Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Samueli 7:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Ndiyeno mfumuyo inauza mneneri Natani+ kuti: “Ine ndikukhala mʼnyumba ya mitengo ya mkungudza,+ pamene Likasa la Mulungu woona likukhala mutenti.”+

  • 1 Mafumu 8:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Ndipo bambo anga Davide ankafunitsitsa kumanga nyumba ya dzina la Yehova Mulungu wa Isiraeli.+

  • 1 Mbiri 15:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Ndiyeno Davide anasonkhanitsa Aisiraeli onse ku Yerusalemu kuti akanyamule Likasa la Yehova, kupita nalo kumalo amene iye anakonza kuti akaliike.+

  • 1 Mbiri 15:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Ndiyeno anawauza kuti: “Inuyo ndinu atsogoleri a nyumba za makolo a Alevi. Choncho inu ndi abale anu mudziyeretse ndipo mukatenge Likasa la Yehova Mulungu wa Isiraeli nʼkukaliika kumalo amene ndakonza kuti lizikhalako.

  • Machitidwe 7:45, 46
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 45 Makolo athu analandira chihemachi kwa makolo awo ndipo analowa nacho limodzi ndi Yoswa mʼdziko limene munali anthu a mitundu ina.+ Anthu amenewa Mulungu anawathamangitsa pamaso pa makolo athu+ ndipo chihemacho chinakhala mʼdzikoli mpaka nthawi ya Davide. 46 Mulungu anakomera mtima Davide ndipo iye anapempha mwayi woti amange nyumba yoti Mulungu wa Yakobo azikhalamo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena