-
Numeri 21:21-24Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
21 Tsopano Aisiraeli anatuma anthu kuti apite kwa Sihoni mfumu ya Aamori kukanena kuti:+ 22 “Tiloleni tidutse mʼdziko lanu. Sitikhotera mʼmunda uliwonse kapena mʼmunda wa mpesa. Sitimwa madzi pachitsime chilichonse. Tizingoyenda mu Msewu wa Mfumu mpaka titadutsa mʼdziko lanu.”+ 23 Koma Sihoni sanalole kuti Aisiraeli adutse mʼdziko lake. Mʼmalomwake, iye anasonkhanitsa anthu ake onse nʼkupita kukamenyana ndi Aisiraeli mʼchipululumo. Anakafika ku Yahazi ndipo anayamba kumenyana ndi Aisiraeli.+ 24 Koma Aisiraeli anapha anthuwo ndi lupanga+ nʼkuwalanda dziko lawo,+ kuyambira kuchigwa cha Arinoni+ mpaka kuchigwa cha Yaboki,+ pafupi ndi Aamoni, chifukwa Yazeri+ anachita malire ndi Aamoni.+
-