5 Chifukwa inu Yehova, Mulungu wa magulu ankhondo akumwamba, ndinu Mulungu wa Isiraeli.+
Nyamukani ndipo muone zimene mitundu yonse ya anthu ikuchita.
Musasonyeze chifundo kwa aliyense woipa komanso wachiwembu.+ (Selah)
6 Amabwera madzulo aliwonse.+
Amauwa ngati agalu+ ndipo amazungulira mzinda wonse.+