Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ezara 1:1, 2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 1 Mʼchaka choyamba cha Koresi+ mfumu ya Perisiya, pokwaniritsa mawu a Yehova amene analankhula kudzera mwa Yeremiya,+ Yehova analimbikitsa Koresi mfumu ya Perisiya kuti alengeze mu ufumu wake wonse, zomwenso iye analemba mʼmakalata,+ kuti:

      2 “Koresi mfumu ya Perisiya wanena kuti, ‘Yehova Mulungu wakumwamba wandipatsa maufumu onse apadziko lapansi.+ Iye wandituma kuti ndimumangire nyumba ku Yerusalemu+ mʼdziko la Yuda.

  • Yesaya 41:25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 Ine ndapatsa mphamvu winawake kuchokera kumpoto, ndipo abwera.+

      Iye adzachokera kotulukira dzuwa*+ ndipo adzaitana pa dzina langa.

      Adzapondaponda olamulira* ngati akuponda dongo+

      Ngati woumba amene amapondaponda dongo laliwisi.

  • Yesaya 45:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 45 Izi ndi zimene Yehova akunena kwa wodzozedwa wake, kwa Koresi,+

      Amene wamugwira dzanja lake lamanja+

      Kuti agonjetse mitundu ya anthu pamaso pake,+

      Kuti alande zida zankhondo za mafumu,*

      Kuti amutsegulire zitseko zokhala ziwiriziwiri,

      Kuti mageti adzakhale osatseka. Iye wamuuza kuti:

  • Yesaya 46:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Ine ndikuitana mbalame yodya nyama kuchokera kotulukira dzuwa,*+

      Ndikuitana munthu kuchokera kudziko lakutali kuti adzachite zolinga zanga.+

      Ineyo ndalankhula ndipo ndidzazichita.

      Ndakonza kuti zimenezi zichitike komanso ndidzazichita.+

  • Danieli 10:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Mʼchaka chachitatu cha ulamuliro wa Mfumu Koresi+ ya Perisiya, Mulungu anamuululira nkhani inayake Danieli, amene ankadziwikanso ndi dzina lakuti Belitesazara.+ Nkhani imene anauzidwayo inali yoona ndipo inali yokhudza nkhondo yaikulu. Danieli anamvetsa nkhani imeneyi ndipo anathandizidwa kumvetsa zinthu zimene anaonazo.

Mabuku a Chichewa (1974-2026)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena