11 Aroni azibweretsa ngʼombe yamphongo ya nsembe yake yamachimo, ndipo aziphimba machimo ake ndi a banja lake. Pambuyo pake azipha ngʼombe ya nsembe yake yamachimoyo.+
27 Mosiyana ndi akulu a ansembe ena, iye safunikira kupereka tsiku ndi tsiku nsembe+ za machimo ake choyamba, kenako za anthu ena.+ Zili choncho chifukwa iye anadzipereka kamodzi kokha kuti akhale nsembe yothandiza anthu mpaka kalekale.+