-
Yesaya 2:3, 4Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 Anthu ochokera mʼmitundu yosiyanasiyana adzabwera nʼkunena kuti:
“Bwerani. Tiyeni tipite kukakwera phiri la Yehova,
Tipite kunyumba ya Mulungu wa Yakobo.+
Iye akatiphunzitsa njira zake,
Ndipo ife tidzayenda mʼnjira zakezo.”+
Chifukwa chilamulo chidzaphunzitsidwa* mu Ziyoni,
Ndipo mawu a Yehova adzaphunzitsidwa mu Yerusalemu.+
4 Mulungu adzaweruza anthu a mitundu yosiyanasiyana
Ndipo adzakonza zinthu zimene ndi zolakwika pakati pawo.
Iwo adzasula malupanga awo kuti akhale makasu a pulawo,
Ndipo mikondo yawo adzaisula kuti ikhale zida zosadzira mitengo.+
Mtundu wa anthu sudzanyamula lupanga kuti umenyane ndi mtundu unzake,
Ndipo anthuwo sadzaphunziranso nkhondo.+
-
-
Yesaya 11:6-9Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
6 Mmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wa nkhosa kwa kanthawi,+
Ndipo kambuku adzagona pansi ndi mbuzi yaingʼono,
Mwana wa ngʼombe, mkango wamphamvu ndi nyama yonenepa zidzakhala pamodzi,*+
Ndipo kamnyamata kakangʼono kadzazitsogolera.
7 Ngʼombe ndi chimbalangondo zidzadyera pamodzi
Ndipo ana awo adzagona pansi pamodzi.
Mkango udzadya udzu ngati ngʼombe yamphongo.+
8 Mwana woyamwa adzasewera pa una wa mamba,
Ndipo mwana amene anasiya kuyamwa adzapisa dzanja lake kudzenje la njoka yapoizoni.
-
-
Mika 4:2Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
2 Anthu ochokera mʼmitundu yosiyanasiyana adzabwera nʼkunena kuti:
“Bwerani, tiyeni tipite kuphiri la Yehova,
Tipite kunyumba ya Mulungu wa Yakobo.+
Iye akatiphunzitsa njira zake,
Ndipo ife tidzayenda mʼnjira zakezo.”
Chifukwa chilamulo,* chidzaphunzitsidwa mu Ziyoni
Ndipo mawu a Yehova adzaphunzitsidwa mu Yerusalemu.
-