Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesaya 2:3, 4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  3 Anthu ochokera mʼmitundu yosiyanasiyana adzabwera nʼkunena kuti:

      “Bwerani. Tiyeni tipite kukakwera phiri la Yehova,

      Tipite kunyumba ya Mulungu wa Yakobo.+

      Iye akatiphunzitsa njira zake,

      Ndipo ife tidzayenda mʼnjira zakezo.”+

      Chifukwa chilamulo chidzaphunzitsidwa* mu Ziyoni,

      Ndipo mawu a Yehova adzaphunzitsidwa mu Yerusalemu.+

       4 Mulungu adzaweruza anthu a mitundu yosiyanasiyana

      Ndipo adzakonza zinthu zimene ndi zolakwika pakati pawo.

      Iwo adzasula malupanga awo kuti akhale makasu a pulawo,

      Ndipo mikondo yawo adzaisula kuti ikhale zida zosadzira mitengo.+

      Mtundu wa anthu sudzanyamula lupanga kuti umenyane ndi mtundu unzake,

      Ndipo anthuwo sadzaphunziranso nkhondo.+

  • Yesaya 11:6-9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  6 Mmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wa nkhosa kwa kanthawi,+

      Ndipo kambuku adzagona pansi ndi mbuzi yaingʼono,

      Mwana wa ngʼombe, mkango wamphamvu ndi nyama yonenepa zidzakhala pamodzi,*+

      Ndipo kamnyamata kakangʼono kadzazitsogolera.

       7 Ngʼombe ndi chimbalangondo zidzadyera pamodzi

      Ndipo ana awo adzagona pansi pamodzi.

      Mkango udzadya udzu ngati ngʼombe yamphongo.+

       8 Mwana woyamwa adzasewera pa una wa mamba,

      Ndipo mwana amene anasiya kuyamwa adzapisa dzanja lake kudzenje la njoka yapoizoni.

       9 Sizidzavulazana+

      Kapena kuwonongana mʼphiri langa lonse loyera,+

      Chifukwa dziko lapansi lidzadzaza ndi anthu odziwa Yehova

      Ngati mmene madzi amadzazira mʼnyanja.+

  • Mika 4:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  2 Anthu ochokera mʼmitundu yosiyanasiyana adzabwera nʼkunena kuti:

      “Bwerani, tiyeni tipite kuphiri la Yehova,

      Tipite kunyumba ya Mulungu wa Yakobo.+

      Iye akatiphunzitsa njira zake,

      Ndipo ife tidzayenda mʼnjira zakezo.”

      Chifukwa chilamulo,* chidzaphunzitsidwa mu Ziyoni

      Ndipo mawu a Yehova adzaphunzitsidwa mu Yerusalemu.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena