-
2 Mbiri 36:15, 16Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
15 Yehova Mulungu wa makolo awo anapitiriza kuwachenjeza kudzera mwa atumiki ake. Ankawachenjeza mobwerezabwereza chifukwa ankamvera chisoni anthu akewo ndiponso malo ake okhala. 16 Koma iwo anapitiriza kunyoza atumiki a Mulungu woona,+ kunyoza mawu ake+ ndiponso kuseka aneneri ake.+ Iwo anafika poti panalibenso chiyembekezo choti angathe kuchiritsidwa. Kenako Yehova anawakwiyira kwambiri nʼkuwalanga.+
-
-
Yesaya 8:14, 15Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
14 Iye adzakhala ngati malo opatulika,
Koma kwa nyumba zonse ziwiri za Isiraeli,
Adzakhala ngati mwala wopunthwitsa+
Ndiponso ngati thanthwe lokhumudwitsa.
Adzakhala ngati msampha komanso khwekhwe
Kwa anthu okhala mu Yerusalemu.
15 Anthu ambiri pakati pawo adzapunthwa nʼkugwa ndipo adzathyoka.
Iwo adzakodwa nʼkugwidwa.
-