2 Mowabu sakutamandidwanso.
Ku Hesiboni+ adani amukonzera chiwembu kuti amuwononge ndipo akunena kuti:
‘Bwerani, tiyeni timuwononge kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’
Iwenso Madimeni khala chete,
Chifukwa lupanga likukutsatira.
3 Ku Horonaimu+ kwamveka kulira kofuula,
Kwamveka phokoso lachiwonongeko ndi kugwa kwakukulu.