-
Ezekieli 10:9-13Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
9 Pamene ndinkaona masomphenyawo, ndinaona kuti pambali pa akerubiwo panali mawilo 4. Pambali pa kerubi aliyense panali wilo limodzi ndipo mawilowo ankaoneka kuti akuwala ngati mwala wa kulusolito.+ 10 Mawilo 4 onsewo ankaoneka mofanana. Ankaoneka ngati wilo lina lili pakati pa wilo linzake. 11 Mawilowo akamayenda ankatha kulowera kumbali iliyonse pa mbali zonse 4 popanda kutembenuka chifukwa ankatha kupita kumene mitu ya akerubiwo yayangʼana popanda kutembenuka. 12 Mʼmatupi onse a akerubiwo, kumsana kwawo, mʼmanja mwawo, mʼmapiko awo ndiponso mʼmawilo a akerubi onse 4 munali maso paliponse.+ 13 Kenako ndinamva mawu akuitana mawilowo kuti, “Mawilo inu!”
-