-
Yeremiya 28:15, 16Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
15 Kenako mneneri Yeremiya anauza mneneri Hananiya+ kuti: “Tamvera iwe Hananiya! Yehova sanakutume, koma iwe wachititsa anthuwa kukhulupirira zinthu zabodza.+ 16 Choncho Yehova wanena kuti, ‘Ndikukuchotsera moyo wako. Chaka chomwe chino iweyo ufa, chifukwa walimbikitsa anthu kuti apandukire Yehova.’”+
-