Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 20:8-10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Muzikumbukira tsiku la Sabata ndipo muziliona kuti ndi lopatulika.+ 9 Muzigwira ntchito zanu zonse kwa masiku 6.+ 10 Koma tsiku la 7 ndi sabata la Yehova Mulungu wanu. Musamagwire ntchito iliyonse inuyo kapena mwana wanu wamwamuna, mwana wanu wamkazi, kapolo wanu wamwamuna, kapolo wanu wamkazi, chiweto chanu kapena mlendo amene akukhala mumzinda wanu.*+

  • Levitiko 23:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Muzigwira ntchito masiku 6, koma tsiku la 7 likhale sabata lopuma pa ntchito zanu zonse.+ Limeneli ndi tsiku la msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse chifukwa limeneli ndi sabata la Yehova kulikonse kumene mungakhale.+

  • Levitiko 23:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 “Lankhula ndi Aisiraeli, ndipo uwauze kuti, ‘Mʼmwezi wa 7, pa tsiku loyamba la mweziwo, muzipuma pa ntchito zanu zonse. Limeneli ndi tsiku la chikumbutso, ndipo lipenga likalira+ muzisonkhana kuti mulambire Mulungu.

  • Levitiko 25:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Koma mʼchaka cha 7 dzikolo lizidzasunga sabata lopuma pa zonse, sabata la Yehova. Musamadzadzale mbewu mʼminda yanu kapena kudulira mitengo yanu ya mpesa.

  • Levitiko 25:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Chaka cha 50 chidzakhala Chaka cha Ufulu kwa inu. Musadzalime minda yanu kapena kukolola mbewu zomera zokha, kapenanso kukolola mphesa zamʼmitengo yosadulira.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena