-
Yesaya 2:2, 3Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
2 Mʼmasiku otsiriza,
Phiri la nyumba ya Yehova
Lidzakhazikika pamwamba penipeni pa mapiri akuluakulu,+
Ndipo lidzakwezedwa kupitirira mapiri angʼonoangʼono.
Anthu a mitundu yonse adzapita kumeneko.+
3 Anthu ochokera mʼmitundu yosiyanasiyana adzabwera nʼkunena kuti:
“Bwerani. Tiyeni tipite kukakwera phiri la Yehova,
Tipite kunyumba ya Mulungu wa Yakobo.+
Iye akatiphunzitsa njira zake,
Ndipo ife tidzayenda mʼnjira zakezo.”+
-
-
Yesaya 66:20Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
20 Adzabweretsa abale anu onse kuchokera ku mitundu yonse+ ngati mphatso kwa Yehova. Adzawabweretsa atakwera mahatchi, ngolo, ngolo zotseka pamwamba, nyulu* ndi ngamila zothamanga, mpaka kukafika kuphiri langa loyera, ku Yerusalemu. Adzachita zimenezi ngati mmene Aisiraeli amabweretsera mphatso mʼnyumba ya Yehova, ataiika mʼchiwiya choyera,” akutero Yehova.
-