16 Koma inu ndinu osangalala chifukwa maso anu amaona komanso makutu anu amamva.+ 17 Chifukwa ndithu ndikukuuzani, aneneri ambiri komanso anthu olungama ankalakalaka kuti aone zinthu zimene mukuziona inuzi koma sanazione,+ komanso kuti amve zimene mukumva inuzi koma sanazimve.