3 “Taonani! Ine ndikutumiza mthenga wanga ndipo adzandikonzera njira.+ Mwadzidzidzi, Ambuye woona, amene anthu inu mukumufunafuna, adzabwera kukachisi wake.+ Ndiponso mthenga wa pangano amene mukumuyembekezera mosangalala adzabwera. Iye adzabwera ndithu,” watero Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.