Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 3:1-3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Mʼmasiku amenewo, Yohane+ Mʼbatizi anapita mʼchipululu cha Yudeya nʼkuyamba kulalikira.+ 2 Iye ankalalikira kuti: “Lapani, chifukwa Ufumu wakumwamba wayandikira.”+ 3 Mneneri Yesaya ananeneratu za iyeyu+ mʼmawu awa: “Winawake akufuula mʼchipululu kuti: ‘Konzani njira ya Yehova!* Muwongole misewu yake.’”+

  • Mateyu 11:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Pamene ophunzira a Yohane ankabwerera, Yesu anayamba kuuza gulu la anthu za Yohane kuti: “Kodi munapita mʼchipululu kukaona chiyani?+ Kodi munapita kukaona bango logwedezeka ndi mphepo?+

  • Mateyu 11:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Malemba amanena za iyeyu kuti: ‘Taona! Ine ndikutumiza mthenga wanga kuti atsogole kukakukonzera njira!’+

  • Maliko 1:2-4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Mogwirizana ndi zimene zinalembedwa mʼbuku la mneneri Yesaya kuti: “(Taona! Ine ndikutumiza mthenga wanga kuti atsogole* kukakukonzera njira.)*+ 3 Winawake akufuula mʼchipululu kuti: ‘Konzani njira ya Yehova!* Muwongole misewu yake.’”+ 4 Yohane Mʼbatizi anali mʼchipululu ndipo ankalalikira za ubatizo monga chizindikiro cha kulapa kuti machimo akhululukidwe.+

  • Luka 1:76
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 76 Koma kunena za mwana wamngʼonowe, udzatchedwa mneneri wa Wamʼmwambamwamba, chifukwa udzatsogola pamaso pa Yehova* kuti ukakonze njira zake.+

  • Yohane 1:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Kunabwera munthu wina amene anatumidwa monga nthumwi ya Mulungu. Dzina lake anali Yohane.+

  • Yohane 1:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Iye anati: “Ndine mawu a winawake amene akufuula mʼchipululu kuti, ‘Wongolani njira ya Yehova,’*+ monga mmene mneneri Yesaya ananenera.”+

  • Yohane 3:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Inunso ndinu mboni pa zimene ndinanena kuti, ‘Ine si Khristu,+ koma ndinatumizidwa monga kalambulabwalo wake.’+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena