Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 3:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Panamvekanso mawu ochokera kumwamba+ onena kuti: “Uyu ndi Mwana wanga+ wokondedwa ndipo amandisangalatsa kwambiri.”+

  • Maliko 9:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Ndiyeno kunachita mtambo umene unawaphimba. Kenako panamveka mawu+ kuchokera mumtambomo akuti: “Uyu ndi Mwana wanga wokondedwa.+ Muzimumvera.”+

  • Yohane 12:28-30
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Atate lemekezani dzina lanu.” Atatero mawu+ anamveka kuchokera kumwamba kuti: “Ndalilemekeza ndipo ndidzalilemekezanso.”+

      29 Choncho gulu la anthu amene anali ataimirira pamenepo anamva zimenezi ndipo anayamba kunena kuti kwagunda bingu. Ena ankanena kuti: “Mngelo walankhula naye.” 30 Yesu anawauza kuti: “Mawu amenewa sanamveke chifukwa cha ine, koma chifukwa cha inu.

  • 1 Yohane 5:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Nʼzoona kuti timakhulupirira umboni umene anthu amapereka, komatu umboni umene Mulungu amapereka ndi woposa umboni umenewo. Choncho timakhulupirira umboni umene Mulungu amapereka wokhudza Mwana wake.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena