Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesaya 26:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 “Anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo.

      Anthu anga amene anafa adzadzuka* nʼkuimirira.+

      Dzukani ndipo mufuule mosangalala,

      Inu anthu okhala mʼfumbi!+

      Chifukwa mame anu ali ngati mame amʼmawa,*

      Ndipo dziko lapansi lidzatulutsa anthu amene anafa kuti akhalenso ndi moyo.*

  • Yohane 5:28, 29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Musadabwe nazo zimenezi, chifukwa nthawi ikubwera imene onse amene ali mʼmanda achikumbutso adzamva mawu ake+ 29 ndipo adzatuluka. Amene ankachita zabwino adzauka kuti alandire moyo ndipo amene ankachita zoipa adzauka kuti aweruzidwe.+

  • Machitidwe 24:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Ndipo ine ndili ndi chiyembekezo ngati chimenenso anthu awa ali nacho, kuti Mulungu adzaukitsa+ olungama ndi osalungama omwe.+

  • Aheberi 11:35
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 35 Akazi analandira anthu akufa amene anaukitsidwa.+ Koma anthu ena anazunzidwa chifukwa sanalole kusiya chikhulupiriro chawo kuti amasulidwe. Iwo anachita zimenezi kuti adzaukitsidwe pa kuuka kwabwino kwambiri.

  • Chivumbulutso 20:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Ndiye ndinaona akufa, olemekezeka ndi onyozeka, ataimirira pamaso pa mpando wachifumuwo, ndipo mipukutu inatambasulidwa. Koma panali mpukutu wina umene unatambasulidwa, womwe ndi mpukutu wa moyo.+ Akufa anaweruzidwa potengera zimene zinalembedwa mʼmipukutuyo, mogwirizana ndi ntchito zawo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena