Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Machitidwe 4:29, 30
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Koma tsopano Yehova,* imvani mmene akutiopsezera ndipo tithandizeni ife akapolo anu kuti tipitirize kulankhula mawu anu molimba mtima. 30 Pitirizani kuchiritsa anthu ndi dzanja lanu komanso kuthandiza kuti zodabwitsa zipitirize kuchitika+ mʼdzina la Yesu, mtumiki wanu woyera.”+

  • Machitidwe 6:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Sitefano anali ndi mphamvu ndipo ankachita kuonekeratu kuti Mulungu ali naye. Iye ankachita zinthu zodabwitsa ndi zizindikiro zazikulu pakati pa anthu.

  • Machitidwe 14:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Choncho kwa nthawi yaitali, ankalankhula molimba mtima chifukwa cha mphamvu ya Yehova.* Iye anatsimikizira mawu a kukoma mtima kwake kwakukulu, polola kuti ophunzirawo azichita zizindikiro ndi zodabwitsa.+

  • Machitidwe 15:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Zitatero gulu lonselo linakhala chete, ndipo linayamba kumvetsera pamene Baranaba ndi Paulo ankafotokoza zizindikiro ndi zodabwitsa zambiri zimene Mulungu anachita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mwa iwo.

  • Aroma 15:18, 19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Sindidzalankhula chilichonse chimene ndachita pandekha, koma zokhazo zimene Khristu wachita ndi kulankhula kudzera mwa ine kuti ndithandize anthu a mitundu ina kukhala omvera. 19 Iwo akhala omvera chifukwa cha zodabwitsa zamphamvu ndiponso zizindikiro+ zimene mzimu wa Mulungu wachita. Choncho ndalalikira mokwanira uthenga wabwino wonena za Khristu kuyambira ku Yerusalemu mpaka ku Iluriko.+

  • 2 Akorinto 12:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Ndithudi inuyo munaona umboni wakuti ndine mtumwi. Munaona kuti ndinapirira kwambiri,+ ndinachita zizindikiro, zinthu zodabwitsa ndiponso ntchito zamphamvu.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena