19 ndiponso pogwiritsa ntchito mphamvu yochita zizindikiro ndi zinthu zodabwitsa zolosera zam’tsogolo,+ mwa mphamvu ya mzimu woyera. Chotero ndalalikira mokwanira uthenga wabwino wonena za Khristu+ kuyambira ku Yerusalemu, kuzungulira+ mpaka ku Iluriko.