Machitidwe 19:22 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 22 Choncho ku Makedoniya anatumizako awiri mwa anthu amene ankamutumikira, omwe ndi Timoteyo+ ndi Erasito.+ Koma iye anakhalabe mʼchigawo cha Asia kwa kanthawi ndithu. Aroma 16:21 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 21 Wantchito mnzanga Timoteyo akupereka moni, chimodzimodzinso Lukiyo, Yasoni ndi Sosipato omwe ndi achibale anga.+ 1 Akorinto 4:17 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 17 Nʼchifukwa chake ndikukutumizirani Timoteyo, popeza iye ndi mwana wanga wokondedwa ndiponso wokhulupirika mwa Ambuye. Iye adzakukumbutsani mmene ndimachitira zinthu potumikira Khristu Yesu+ komanso mmene ndimaphunzitsira kulikonse, mumpingo uliwonse. 1 Atesalonika 3:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Ndiye tinatumiza Timoteyo+ mʼbale wathu, yemwe ndi mtumiki wa Mulungu* amene akulengeza uthenga wabwino wonena za Khristu. Tinamutumiza kuti adzakulimbikitseni ndi kukutonthozani nʼcholinga choti chikhulupiriro chanu chikhale cholimba. 1 Timoteyo 1:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Ndikukulembera iwe Timoteyo,*+ mwana wanga weniweni+ mʼchikhulupiriro: Mulungu Atate wathu ndi Khristu Yesu Ambuye wathu akupatse kukoma mtima kwakukulu, chifundo ndi mtendere.
22 Choncho ku Makedoniya anatumizako awiri mwa anthu amene ankamutumikira, omwe ndi Timoteyo+ ndi Erasito.+ Koma iye anakhalabe mʼchigawo cha Asia kwa kanthawi ndithu.
21 Wantchito mnzanga Timoteyo akupereka moni, chimodzimodzinso Lukiyo, Yasoni ndi Sosipato omwe ndi achibale anga.+
17 Nʼchifukwa chake ndikukutumizirani Timoteyo, popeza iye ndi mwana wanga wokondedwa ndiponso wokhulupirika mwa Ambuye. Iye adzakukumbutsani mmene ndimachitira zinthu potumikira Khristu Yesu+ komanso mmene ndimaphunzitsira kulikonse, mumpingo uliwonse.
2 Ndiye tinatumiza Timoteyo+ mʼbale wathu, yemwe ndi mtumiki wa Mulungu* amene akulengeza uthenga wabwino wonena za Khristu. Tinamutumiza kuti adzakulimbikitseni ndi kukutonthozani nʼcholinga choti chikhulupiriro chanu chikhale cholimba.
2 Ndikukulembera iwe Timoteyo,*+ mwana wanga weniweni+ mʼchikhulupiriro: Mulungu Atate wathu ndi Khristu Yesu Ambuye wathu akupatse kukoma mtima kwakukulu, chifundo ndi mtendere.