17 Musalakelake nyumba ya mnzanu. Musalakelake mkazi wa mnzanu,+ kapolo wake wamwamuna, kapolo wake wamkazi, ngʼombe yake yamphongo, bulu wake, kapena chinthu chilichonse cha mnzanu.”+
21 Musalakelake mkazi wa mnzanu.+ Musalakelake mwadyera nyumba ya mnzanu, munda wake, kapolo wake wamwamuna, kapolo wake wamkazi, ngʼombe yake yamphongo, bulu wake, kapena chinthu chilichonse cha mnzanu.’+