19 Tikudziwa kuti zinthu zonse zimene Chilamulo chimanena zimagwira ntchito kwa amene amatsatira Chilamulo. Cholinga chake nʼkuchititsa anthu kuti asowe chonamizira komanso kusonyeza kuti dziko lonse lili ndi mlandu pamaso pa Mulungu ndipo ndi loyenera kulandira chilango.+