Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 51:7, 8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Babulo anali ngati kapu yagolide mʼdzanja la Yehova.

      Anachititsa kuti dziko lonse lapansi liledzere.

      Mitundu ya anthu yaledzera ndi vinyo wake.+

      Nʼchifukwa chake mitundu ya anthu ikuchita zinthu ngati anthu amisala.+

       8 Babulo wagwa mwadzidzidzi ndipo wasweka.+

      Mulirireni mofuula.+

      Mʼpatseni mafuta a basamu kuti ululu wake uthe, mwina angachire.”

  • Chivumbulutso 17:1, 2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Mmodzi wa angelo 7 amene anali ndi mbale 7 aja,+ anabwera nʼkundiuza kuti: “Bwera, ndikuonetse chiweruzo cha hule lalikulu limene lakhala pamadzi ambiri,+ 2 limene mafumu a dziko lapansi anachita nalo chiwerewere,*+ ndipo linaledzeretsa anthu amene akukhala padziko lapansi ndi vinyo wa chiwerewere* chake.”+

  • Chivumbulutso 18:2, 3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Iye anafuula ndi mawu amphamvu akuti: “Wagwa! Babulo Wamkulu wagwa,+ ndipo wakhala malo amene ziwanda zimakhala. Wakhalanso malo amene mzimu uliwonse wonyansa* komanso mbalame iliyonse yonyansa ndi imene imadedwa zimabisala.+ 3 Iye wamwetsa mitundu yonse ya anthu vinyo wa chilakolako chake cha* chiwerewere.*+ Ndipo mafumu a dziko lapansi anachita naye chiwerewere.+ Amalonda* apadziko lapansi analemera chifukwa cha zinthu zambiri zamtengo wapatali zimene mkazi ameneyu anadziunjikira mopanda manyazi.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena