Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g87 12/8 tsamba 31
  • “Chitetezero cha Thanzi Langa”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • “Chitetezero cha Thanzi Langa”
  • Galamukani!—1987
Galamukani!—1987
g87 12/8 tsamba 31

“Chitetezero cha Thanzi Langa”

Ndizo zimene wolembetsa wina wa ku Senegal, West Africa, adanena za magazini ya Galamukani! Iye analemba kuti:

“Ndiri wosangalala kwambiri kuti ndimaŵerenga Galamukani! nthaŵi zonse chifukwa cha nkhani zabwino kwambiri zimene imasimba. Zoyenerera ndendende ndipo zofunika kwambiri kaamba ka tsiku lathu lamakono. Ndine wolembetsa kwa zaka ziŵiri ndi theka. Kudzera m’kalatayi ndikufuna kuyamikira alembi ndi ofalitsa kaamba ka thandizo lawo ku chitetezero cha thanzi langa, ndipo osati langa lokha komanso la ena ambiri omwe akhala okhoza kuleka zizoloŵezi za fodya ndi kutetezera thanzi la iwo eni mwakupeza nyonga yofunika kudzera m’kuŵerenga nkhani za mu Galamukani! Chonde pitirizani kukonzekera nkhani zonena za maupandu a fodya, popeza kuti ndikupeza kuti mbali zitatu za zinayi za achichepere amene ndimakhala nawo amasuta fodya, imene iri yaupandu osati ku thanzi lawo lokha ndi la ena komanso kuwononga ndalama zawo. Ndiyamikira kaamba ka zonse zimene ndimapeza poŵerenga magazini anu.”

Tiganiza kuti inu, nanunso, mudzapindula mwakuŵerenga Galamukani! Landirani kulembetsa kwa chaka chimodzi mwakungolemba ndi kutumiza kapepala kotsatirapoka limodzi ndi K16.00 yokha.

Chonde tumizani kulembetsa kwa chaka chimodzi kwa Galamukani! Ndatsekeramo K16.00 kaamba ka makope 12 a magazini imeneyi (kope imodzi pa mwezi).

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena