‘Monga Mkate ndi Madzi ku Mtima’
Mmenemo ndi mmene magazine a Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! anawonedwera ndi minisitala Wachiprotestanti kuchokera ku Málaga, Spanya. Iye analongosola kuti:
“Ndakhala pasitala Wachiprotestanti kwa zaka zambiri, ndipo ndingakutsimikizireni kuti m’maphunziro anga onse a zaumulungu, sindinapeze kufupikitsidwa ndi kumvekera kumene zofalitsidwa zanu ziri nako. Kwa ine, Mboni za Yehova ali anthu okhumbirika; m’dziko la chinyengo, iwo amakhala molingana ndi chimene iwo amakhulupirira. . . .
“Pa nthaŵi ino, chifukwa cha mavuto aumwini, sindingaphunzire ndi inu, monga mmene ndingakhumbire, koma ndiyamikira Mulungu kuti, ndimalandira magazine anu, ndipo ali ‘mkate’ ndi ‘madzi’ ku mtima wanga, womwe umamva njala ndi ludzu kaamba ka Mulungu wa moyo.”
Inu nanunso mungakhale ndi Nsanja ya Olonda ndi magazine anzake, Galamukani!, ataperekedwa kunyumba kwanu mwa kudzaza ndi kutumiza kapepala kotsatiraka.
Chonde tumizani kulembetsa kwa chaka chimodzi kwa Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! Ndatsekeramo K120 (Zambia).