Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g90 11/8 tsamba 32
  • “Bokosi la Chuma cha Mafunso ndi Mayankho”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • “Bokosi la Chuma cha Mafunso ndi Mayankho”
  • Galamukani!—1990
Galamukani!—1990
g90 11/8 tsamba 32

“Bokosi la Chuma cha Mafunso ndi Mayankho”

Umu ndimmene mkazi wa ku Pittsburgh, Pennsylvania, U.S.A., analitchela bukhu lakumanja la Kukambitsirana za m’Malemba. Iye analongosola kuti: “Posachedwapa Mboni za Yehova ziŵiri zinabwera panyumba panga. . . . Mmodzi wa iwo mosadziŵa anasiya bukhu lamutu wakuti Kukambitsirana za m’Malemba. Kunena zowona, ndinamwerekera m’bukhulo! Ndinakhala pansi ndikuliŵerenga kwa maola ambiri. Ndinasangalatsidwa kwenikweni. . . . Bukhuli linali ngati bokosi la chuma cha mafunso ndi mayankho kwa ine, ambiri amene ndadzifunsapo ndekha.”

Bukhu la kumanja lofunika kwambiri limeneli njodzala ndi mitu yaikulu yoposa 70. Kuphatikizapo “Kutaya Mimba,” “Mankhwala,” “Maholide,” “Kutengedwa m’Thupi,” “Kudziveka Thupi Lanyama,” “Kugonana,” ndi “Kulambira Mizimu.” Zisonyezero zake za nkhani zamasamba asanu ndi aŵiri ndi malemba zingakuthandizeni kupeza mayankho mofulumira. Kuti mulandire kope, chonde dzazani ndikutumiza kapepala kali pansipa.

Ndingakonde kulandira bukhu lachikuto cholimba, lamasamba 448 la Kukambitsirana za m’Malemba. (Kunja kwa Zambia, lemberani nthambi ya Watch Tower yakwanuko kaamba ka chidziŵitso. Onani tsamba 4.)

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena