Mmene Ukwati Wina Unapulumutsidwira
“Kugwiritsira ntchito uphungu wa m’bukhu la Kupangitsa Moyo Wanu wa Banja Kukhala Wachimwemwe kunapulumutsa ukwati wanga,” analemba motero woŵerenga woyamikira wa ku South Africa. “Mutu 5, ‘Mkazi Amene Ali Wokondedwa Kwambiri,’ unatsegula maso anga. Sindinaganizirepo konse m’maloto anga oipa kuti ndingachititse mavuto ambiri chotero popanda kulingalira. Ndikuyamikani kwabasi. Ukwati wanga unali m’mbali za namondwe zenizeni za nyanja, ndipo tsopano, pambuyo pa miyezi ingapo, wabwereranso ku doko labata lachimwemwe.”
Ngati mufuna thandizo m’kupangitsa ukwati wanu kukhala wachimwemwe koposapo, mungapindule ndi bukhu limeneli. Landirani kope mwakungodzaza ndi kutumiza kapepalaka.
Chonde nditumizani bukhu lachikuto cholimba lamasamba 192 Kupangitsa Moyo Wanu wa Banja Kukhala Wachimwemwe. (Kunja kwa Zambia, lemberani nthambi ya Watch Tower yakwanuko kaamba ka chidziŵitso. Onani tsamba 5.)