Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g93 3/8 tsamba 25
  • Kulinganiza Banja Kukukhala Nkhani ya Padziko Lonse

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kulinganiza Banja Kukukhala Nkhani ya Padziko Lonse
  • Galamukani!—1993
  • Nkhani Yofanana
  • Ana—Kodi Ndiwo Mapindu Kapena Mavuto?
    Galamukani!—1993
  • Makolo Ayenera Kuphunzitsa Ana Awo Kukonda Yehova
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
  • Kodi N’chifukwa Chiyani Alibe Ana?
    Nsanja ya Olonda—2000
  • Nkhani ya Chiŵerengero cha Anthu, M’Baibulo, ndi M’tsogolo
    Galamukani!—2004
Onani Zambiri
Galamukani!—1993
g93 3/8 tsamba 25

Kulinganiza Banja Kukukhala Nkhani ya Padziko Lonse

“Kulinganiza banja kungabweretse mapindu owonjezereka kwa anthu owonjezereka pamtengo wotsika koposa ‘luso la zopangapanga’ limodzi lirilonse limene tsopano liri lopezeka kufuko la anthu. . . . Zimenezi zingakhalebe zowona ngakhale ngati panalibe chinthu chotchedwa kuti vuto la kuchuluka kwa anthu.”—The State of the World’s Children 1992.

M’NTHAŴI zapita kunali kulingaliridwa kukhala kolakalakika kukhala ndi ana ambiri. Pafupifupi zaka zikwi zinayi zapitazo, pamene Rebeka anali pafupi kuchoka ku Mesopotamiya kukakwatibwa ndi Isake, amake ndi mbale wake anamdalitsa mwamawu akuti: “Mlongo wathu ndiwe, iwe ukhale amayi wa anthu zikwizikwi.” (Genesis 24:60) Nthaŵi zasintha. Lerolino, akazi owonjezerekawonjezereka akunena kuti akufuna ana ocheperapo.

“Ndinali wachitatu mwa ana asanu ndi aŵiri,” anatero Bu, mayi wazaka 22 zakubadwa wa ku Indonesia wokhala ndi mwana mmodzi wamkazi. “Atate anali wopanga ndi kugulitsa uchema m’Klaten, Central Java, ndipo makolo anga anavutika kwambiri kuyesayesa kulera ana ambiri chotero. . . . Nkosavutirapo kulera banja ngati uli ndi ana oŵerengeka chabe.”

Mawu a Bu ngofanana ndi a makolo kuzungulira padziko lonse. Mowonjezerekawonjezereka, okwatirana amafuna kulinganiza nthaŵi ya kuyamba kukhala ndi ana, chiŵerengero chawo, mpata wa kusiyana kwa misinkhu, ndi nthaŵi ya kuleka. Zimenezi zikusonyezedwa m’ziŵerengero za UN zosonyeza kuti kugwiritsira ntchito modzifunira njira zopewera kutenga mimba m’maiko osatukuka kwakula kwambiri, kuyambira pa 10 peresenti ya okwatirana mu ma 1960 kufikira ku 51 peresenti lerolino.

Maboma nawonso ali okondweretsedwa mwapadera m’kupititsa patsogolo kulinganiza banja. Yoposa theka ya maiko osatukuka akuchita maprogramu ochepetsa kukula kwa chiŵerengero cha anthu. Population Fund ya gulu la UN likuyerekezera kuti chiwonkhetso cha ndalama zowonongedwera pa maprogramu olamulira chiŵerengero cha anthu tsopano ndicho pafupifupi U.S.$4,500,000,000 pachaka. Kuti afikire zofunika zamtsogolo, akatswiriwo akuyerekezera kuti chiŵerengerochi chidzaŵirikiza podzafika chaka cha 2000.

Kodi nchifukwa ninji maiko ndi anthu paokha ali okondwerera kwambiri kuchepetsa milingo ya kubala ana? Ndipo kodi lingaliro Lachikristu nlotani pankhani yofunika imeneyi? Nkhani ziŵiri zotsatirapozi zidzalingalira mafunso ameneŵa.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena