Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g94 10/8 tsamba 32
  • Mankhwala a Vuto la Kusankhana Mafuko

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mankhwala a Vuto la Kusankhana Mafuko
  • Galamukani!—1994
Galamukani!—1994
g94 10/8 tsamba 32

Mankhwala a Vuto la Kusankhana Mafuko

Posachedwapa mwamuna wina wa ku Oklahoma, U.S.A., analandira kope la magazini a Galamukani! limene linali ndi nkhani yakuti “Kodi Mafuko Onse Adzagwirizana Konse?” Poyamba kulemba kalata yakeyo ndi mawu akuti “Afalitsi a Watchtower Okondedwa,” munthuyo analemba kuti:

“Ndinali ndi mwaŵi wabwino wa kuŵerenga kope lanu la Galamukani! la September 8, 1993, posachedwapa, losimba za vuto la maunansi a mafuko. Ndinadabwa, ndipo ndinachita chidwi, ndi kufotokoza kwanu kosakondera ndi kuzindikira kwanzeru pa vuto locholoŵana limeneli.

“Ndamaliza kosi ya mbiri ya United States pakoleji posachedwapa. Koma m’masamba 9 okha a magazini anu munapereka mbiri yaifupi, mafotokozedwe, NDI MANKHWALA a vuto lobisika limeneli amene akupambana a maphunziro onse a m’mabuku a kukoleji a miyezi isanu ndi umodzi. Nkhani zake zinali zofotokozedwa mosakondera kwakuti nkovuta kudziŵa fuko la olembawo.

“Pamene dziko likhala logaŵanikagaŵanika mowonjezereka chifukwa cha kusankhana mafuko, munthu aliyense afunikira kuŵerenga chidziŵitso cha mtundu umenewu chochuluka chofalitsidwa monga momwe mungathere. Ndikukuthokozani chifukwa cha kukhala kwanu olimba mtima kufalitsa choonadi ndi nzeru yozoloŵereka.”

Ngati mungakonde kuti kope la Galamukani! lizitumizidwa kwanu, chonde lemberani ku Watch Tower, Box 33459, Lusaka, kapena ku keyala yoyenerera yondandalikidwa patsamba 5.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena