Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 11/06 tsamba 9
  • Mulungu Amatiganizira!

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mulungu Amatiganizira!
  • Galamukani!—2006
  • Nkhani Yofanana
  • Dziko Latsopano Lili Pafupi
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2021
  • Mulungu Ndithudi Amakuganizirani
    Nsanja ya Olonda—2004
  • Mungakhale ndi Chiyembekezo M’dziko Lamavutoli
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Kodi Chifuno cha Mulungu cha Dziko Lapansi N’chiyani?
    Kodi Mulungu Amafunanji kwa Ife?
Onani Zambiri
Galamukani!—2006
g 11/06 tsamba 9

Mulungu Amatiganizira!

MMENE Mulungu wachitira ndi nkhani ya kupanduka kwa anthu mu Edene, zikungosonyeza kuti amakonda aliyense wa ife ndipo amaganizira kwambiri za tsogolo lathu. Tikukupemphani kuganizira bwino umboni wotsatirawu wakuti Mulungu amatiganizira, ndipo werengani m’Baibulo lanu malemba amene asonyezedwa.

● Watipatsa dziko lapansi lokongola kwambiri, limene lili ndi zamoyo zosangalatsa, komanso n’lachonde.—Machitidwe 14:17; Aroma 1:20.

● Anapanga thupi lathu modabwitsa kuti tizisangalala ndi moyo m’njira zosiyanasiyana tsiku ndi tsiku, monga kumva kukoma tikamadya chakudya chabwino, kusangalala ndi kulowa kwa dzuwa, kusangalala ndi mwana akamaseka, ndi kumva bwino tikakhala ndi wokondedwa wathu.—Salmo 139:14.

● Watipatsa malangizo anzeru otithandiza kulimbana ndi mavuto osiyanasiyana.—Salmo 19:7, 8; 119:105; Yesaya 48:17, 18.

● Watipatsa chiyembekezo chabwino kwambiri, monga chodzakhala ndi moyo padziko lapansi la paradaiso ndi chodzaona okondedwa athu amene anafa akuukitsidwa.—Luka 23:43; Yohane 5:28, 29.

● Anatumiza Mwana wake wobadwa yekha kudzatifera kuti tikhale ndi chiyembekezo chokhala ndi moyo kosatha.—Yohane 3:16.

● Wakhazikitsa Ufumu wa Mesiya kumwamba n’kutipatsa umboni wokwanira wakuti Ufumu umenewu udzalamulira dziko lapansi posachedwapa.—Yesaya 9:6, 7; Mateyo 24:3, 4, 7; Chivumbulutso 11:15; 12:10.

● Akutipempha kuti tizilankhula naye mwa kupemphera, kumukhuthulira nkhawa zonse za kumtima kwathu, ndipo amatimvetseradi tikamachita zimenezi.—Salmo 62:8; 1 Yohane 5:14, 15.

● Nthawi zonse amatitsimikizira kuti amatikonda ndipo amatidera nkhawa.—1 Yohane 4:9, 10, 19.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena