Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 4/08 tsamba 3
  • Kodi Ndi Masiku Otsiriza a Chiyani?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Ndi Masiku Otsiriza a Chiyani?
  • Galamukani!—2008
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova Alonjeza Danieli Mphotho Yodabwitsa
    Samalani Ulosi wa Danieli!
  • Buku la Danieli ndi Inu
    Samalani Ulosi wa Danieli!
  • Alimbikitsidwa ndi Mthenga Wochokera kwa Mulungu
    Samalani Ulosi wa Danieli!
  • Mfundo Zazikulu za M’buku la Danieli
    Nsanja ya Olonda—2007
Onani Zambiri
Galamukani!—2008
g 4/08 tsamba 3

Kodi Ndi Masiku Otsiriza a Chiyani?

TAYEREKEZERANI kuti pawindo la sitolo ina pali chikwangwani chakuti “Masiku Otsiriza.” Mwina mungaganize kuti nthawi yogulitsa zinthu motchipa yatsala pang’ono kutha kapena sitoloyo aitseka posachedwa. Koma bwanji wina atanena kuti: “Tikukhala m’masiku otsiriza”? Kodi mungati akutanthauza chiyani?

Anthu akhala akugwiritsa ntchito mawu akuti “masiku otsiriza” ndi “nthawi ya chimariziro” kwanthawi yaitali. (2 Timoteyo 3:1; Danieli 12:4) Zaka zoposa 2,500 zapitazo, mneneri Danieli anaona masomphenya a maulamuliro apadziko lapansi ndiponso nkhondo zimene zidzachitike pakati pa maulamulirowo mpaka “nthawi ya chimariziro.” Iye anauzidwa kuti tanthauzo la masomphenya amenewa lidzadziwika bwinobwino panthawi ya chimaliziroyo. (Danieli 8:17, 19; 11:35, 40; 12:9) Danieli analembanso kuti: “Masiku a mafumu aja Mulungu wa Kumwamba adzaika ufumu woti sudzawonongeka ku nthawi zonse, ndi ulamuliro wake sudzasiyidwira mtundu wina wa anthu, koma udzaphwanya ndi kutha maufumu awo onse. Nudzakhala chikhalire.”—Danieli 2:44.

Yesu Khristu anatchula za “mapeto” poyankha funso lokhudza “chizindikiro cha kukhalapo [kwake] ndi cha mapeto a dongosolo lino la zinthu.” (Mateyo 24:3-42) Zikuoneka kuti Danieli komanso Yesu anali kunena za mapeto enaake, kapena kuti kusintha kwa zinthu kumene kudzakhudze anthu onse amene adzakhale ndi moyo ndiponso amene anakhalapo ndi moyo padzikoli. Danieli analemba za kutha kwa maboma onse apadziko lapansi. Yesu ananena za “mapeto a dongosolo lino la zinthu.”

Kodi pali chifukwa choti muziganizira nkhani imeneyi? Inde, chifukwatu munthu aliyense ikumukhudza. Komabe anthu ambiri alibe nayo chidwi nkhani imeneyi. Baibulo linalosera kuti: “M’masiku otsiriza kudzakhala onyodola ndi kunyodola kwawo, otsatira zilakolako zawo, amene azidzati: ‘Kuli kuti kukhalapo kwake kolonjezedwa kuja? Taonani, kuchokera tsiku limene makolo athu anamwalira, zinthu zonse zikupitirirabe chimodzimodzi monga kuyambira pachiyambi cha chilengedwe.’” (2 Petulo 3:3, 4) N’zoona kuti anthu ambiri masiku ano amaona kuti zinthu zikungochitika mmene zakhala zikuchitikira kuyambira kale ndipo amati moyo ukhala chonchi mpaka kalekale.

Kodi pali umboni uliwonse wakuti tilidi m’masiku amene Baibulo limati otsiriza? Tiyeni tione.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena