Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 10/15 tsamba 16
  • Nkhani Zokhudza Mabanja

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Nkhani Zokhudza Mabanja
  • Galamukani!—2015
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Africa
  • Canada
  • Netherlands
  • Makolo Phunzitsani Ana Anu Mwachikondi
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Mungatani Kuti Aliyense Azisangalala M’banja Lanu?​—Mbali Yachiwiri
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Makolo Khalani Chitsanzo Chabwino kwa Ana Anu
    Nsanja ya Olonda—2006
  • Kumanga Banja Lolimba Mwauzimu
    Nsanja ya Olonda—2001
Onani Zambiri
Galamukani!—2015
g 10/15 tsamba 16
Mayi akugwira ntchito pa kompyuta ndipo mwana wake akulira

ZOCHITIKA PADZIKOLI

Nkhani Zokhudza Mabanja

Masiku ano mabanja akukumana ndi mavuto ambiri. Komatu m’Baibulo muli malangizo othandiza kuti mabanja aziyenda bwino.

Africa

Bungwe Loona za Umoyo Padziko Lonse limanena kuti amayi ayenera kuyamba kuyamwitsa ana awo pasanathe ola limodzi mwanayo atangobadwa. Limanenanso kuti ayenera kupitiriza kuyamwitsa mwanayo mwakathithi kwa miyezi 6. Ngakhale kuti bungweli limalimbikitsa zimenezi, nthambi ina ya bungwe la UNICEF yoona za chakudya chopatsa thanzi inanena kuti amalonda akuchititsa anthu kuganiza kuti “mkaka wochita kugula ndi wabwino kwambiri kuposa mkaka wa m’mawere.”

ZIMENE BAIBULO LIMANENA: “Munthu amene sadziwa zinthu amakhulupirira mawu alionse, koma wochenjera amaganizira za mmene akuyendera.”—Miyambo 14:15.

Canada

Akatswiri ena a mumzinda wa Montreal atachita kafukufuku, anapeza kuti ana amene makolo awo amangowapanikiza ndi malamulo okhwima koma osawasonyeza chikondi, akhoza kudzakhala onenepa kwambiri. Ananena kuti pafupifupi ana 30 pa 100 alionse omwe ali ndi makolo oterewa adzakhala ndi vuto lonenepa kwambiri poyerekeza ndi ana omwe makolo awo amapeza nthawi yowalangiza komanso kuwasonyeza kuti amawakonda.

KODI MUKUDZIWA? Baibulo linapereka kalekale malangizo othandiza makolo kulera bwino ana awo.—Akolose 3:21.

Netherlands

Kafukufuku wina amene anachitika m’dzikoli, anasonyeza kuti mabanja amene makolo onse awiri amagwira ntchito, ndipo amagawa bwino nthawi yochita zinthu zakuntchito komanso zapakhomo, amacheza bwino ndi ana awo. Lipotilo linasonyeza kuti izi ndi zosiyana kwambiri ndi makolo omwe sagawa bwino nthawi yawo. Mwachitsanzo, linanena kuti makolo amene amalandira mafoni akuntchito pa nthawi imene ali kunyumba, amalephera kupeza nthawi yocheza ndi ana awo.

TAGANIZIRANI IZI: “Chilichonse chili ndi nthawi yake.”—Mlaliki 3:1.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena