Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 17
  • Amapasa Amene Anali Osiyana

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Amapasa Amene Anali Osiyana
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Yakobo Analandira Madalitso
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Yakobo ndi Esau Akhululukirana
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Muzisankha Zinthu Mwanzeru Kuti Musataye Madalitso Anu
    Nsanja ya Olonda—2013
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 17

NKHANI 17

Amapasa Amene Anali Osiyana

ANYAMATA awiri pano ali osiyana kwambiri, kodi si choncho? Kodi mukudziwa maina ao? Mpalu’yu ndi Esau, ndi mbusa wa nkhosa’yo ndiye Yakobo.

Esau ndi Yabobo anali ana amapasa a Isake ndi Rebeka. Atate’yo, Isake, anakonda kwambiri Esau, chifukwa anali mpalu wabwino ndipo ankadza ndi zakudya za banja’lo. Koma Rebeka anakonda Yakobo kopambana, chifukwa anali mnyamata wofatsa ndi wamtendere.

Gogo Abrahamu anali akali moyo, ndipo tingayerekezere m’mene Yakobo anakondera kumumvetsera akunena za Yehova. Potsiriza Abrahamu anafa ali ndi zaka 175, mapasa’wo ali ndi zaka 15.

Esau ali ndi zaka 40 anakwatira akazi awiri a m’Kanani. Izi zinakwiyitsa kwambiri Isake ndi Rebeka, chifukwa akazi’wa sanalambire Yehova.

Tsiku lina kanthu kena kanachitika kamene kanapsyetsa mtima kwambiri Esau pa mbale wake Yakobo. Nthawi inafika yoti Isake apereke dalitso kwa mwana wake wamkulu. Pakuti Esau anali wamkulu koposa Yakobo, Esau anayembekezera kulandira dalitso’li. Koma Esau anali atagulitsa kuyenera kwa kulandira dalitso’li kwa Yakobo. Ndipo’nso, pa kubadwa kwa ana awiri’wa Mulungu anali atanena kuti Yakobo akalandira dalitso. Ndipo izi ndizo zinachitika. Isake anapereka dalitso’lo kwa mwana wake Yakobo.

Atamva izi Esau anakwiyira Yakobo. Anali wokwiya kwambiri kwakuti anati akapha Yakobo. Atamva izi Rebeka, anada nkhawa kwambiri. Nauza mwamuna wake Isake kuti: ‘Zidzakhala zoopsya’di ngati Yakobo naye’nso akwatira mmodzi wa akazi a Kanani’wa.

Motero anaitana Yakobo mwana wake namuuza kuti: ‘Usakwatire Mkazi wa m’Kanani. Koma upite ku mbumba ya gogo wako Betuele m’Harana. Ukakwatire mmodzi wa ana akazi a mwana wao wamwamuna Labani.’

Yakobo anamvetsera atate wake, pompo ananyamuka kumka kwa abale ake m’Harana.

Genesis 25:5-11, 20-34; 26:34, 35; 27:1-46; 28:1-5; Ahebri 12:16, 17.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena