Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 73
  • Mfumu Yabwino Yomaliza

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mfumu Yabwino Yomaliza
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Yosiya Ankakonda Chilamulo cha Mulungu
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Yosiya Anali ndi Anzake Abwino
    Phunzitsani Ana Anu
  • Yosiya Wodzichepetsayo Anayanjidwa Ndi Yehova
    Nsanja ya Olonda—2000
  • Yosiya Anachita Zabwino
    Nsanja ya Olonda—2009
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 73

NKHANI 73

Mfumu Yabwino Yomaliza

YOSIYA ali ndi zaka zisanu ndi zitatu zokha pamene iye akukhala mfumu ya mafuko awiri a kumwela a Israyeli. Uwu ndi usinkhu wochepa kwambiri woti munthu n’kukhala mfumu. Chotero poyamba anthu achikulire akum’thandiza kulamula mtundu’wo.

Yosiya atakhala mfumu kwa zaka zisanu ndi ziwiri akuyamba kufuna-funa chithandizo cha Yehova. Iye akutsatira chitsanzo cha mafumu abwino onga ngati Davide, Yehosafati ndi Hezekiya. Ndiyeno, akali kamnyamatabe, Yosiya akuchita chinthu chosonyeza kulimba mtima.

Kwa nthawi yaitali Aisrayeli ochuluka akhala oipa kwambiri. Iwo akulambira milungu yonyenga. Iwo akugwadira mafano. Chotero Yosiya akumka ndi amuna ake nayamba kuchotsa kulambira konyenga m’dziko’lo. Iyi n’ntchito yaikulu chifukwa anthu ochuluka akulambira milungu yonyenga. Mungaone Yosiya uyo ndi anthu ake akuphwanya mafano.

Pambuyo pake, iye akuika amuna atatu kuyang’anira ntchito yokonza kachisi. Ndalama zikusonkhedwa kuchokera kwa anthu n’kuperekedwa kwa amuna’wa kuti alipirire ntchito imene iyenera kuchitidwa. Akadagwira ntchito pa kachisi’yo, mkulu wansembe Hilikiya akupeza kanthu kena kofunika kwambiri m’menemo. Ndiro bukhu leni-leni la chilamulo chimene Yehova ananinkha Moses kuchilemba kale-kale’lo. Linali litatayika kwa zaka zambiri.

Bukhu’lo likuperekedwa kwa Yosiya, ndipo iye akupempha am’werengere. Pamene akumvetsera, iye akuona kuti anthu akhala asakusunga chilamulo cha Yehova. Iye akumva nazo chisoni kwambiri, chotero akung’amba zobvala zake, monga momwe mukuonera pano. Iye akuti: ‘Yehova watikwiyira, chifukwa chakuti atate wathu sanasunge malamulo olembedwa m’bukhu’li.

Yosiya akulamula mkulu wa ansembe Hilikiya kupeza zimene Yehova adzawachitira. Hilikiya akumka kwa mkazi’yo Hulida, amene ali mneneri wachikazi, nam’funsa. Iye akum’patsa uthenga uwu wochokera kwa Yehova woti akapereke kwa Yosiya: ‘Yerusalemu ndi anthu onse adzalangidwa chifukwa chakuti iwo alambira milungu yonyenga ndipo dziko’lo ladzazidwa ndi kuipa. Koma chifukwa chakuti iwe, Yosiya, wachita zabwino, chilango ichi sichidzadza kufikira iwe utafa.’

2 Mbiri 34:1-28.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena