Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • yp2 tsamba 97
  • Chitsanzo Chabwino—Lidiya

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chitsanzo Chabwino—Lidiya
  • Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri
  • Nkhani Yofanana
  • Lidiya—Wopembedza Mulungu Ndiponso Wochereza Alendo
    Nsanja ya Olonda—1996
  • Mmene Tingakhalire Osangalala
    Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso
  • “Wolokerani ku Makedoniya Kuno”
    ‘Kuchitira Umboni Mokwanira za Ufumu wa Mulungu’
  • Kodi Ndingatani Kuti Ndikhale Wochezeka?
    Galamukani!—1999
Onani Zambiri
Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri
yp2 tsamba 97

Chitsanzo Chabwino​—Lidiya

Ngakhale kuti Lidiya anali atangokhala kumene wophunzira wa Yesu, iye anaitanira Paulo ndi anzake kunyumba kwake popanda kupemphedwa. (Machitidwe 16:14, 15) N’chifukwa chake anali ndi mwayi wogwirizana ndi Paulo ndiponso anzake aja. Ndipo Paulo ndi Sila atatuluka ku ndende, anapitanso ku nyumba kwa Lidiya—Machitidwe 16:40.

Kodi inunso mungatsatire chitsanzo cha Lidiya poyesetsa kudziwana ndi anthu? Kodi mungachite bwanji zimenezi? Musapupulume. Yambani kulankhula ndi munthu mmodzi. Mukapita ku misonkhano yachikhristu, yesetsani kulankhulana ndi munthu mmodzi m’malo mocheza ndi anthu ambiri nthawi imodzi. Pochezapo muzikhala wansangala. Ngati mukusowa chonena, mufunseni mafunso kapena muuzeni zilizonse zimene zakuchitikirani. Muzimvetsera akamalankhula. M’kupita kwanthawi mudzayamba kulankhula momasuka. Dziwani kuti anthu amakonda kucheza ndi munthu wachifundo ndiponso wokoma mtima. (Miyambo 16:24) Lidiya anapeza anzake abwino chifukwa chakuti anali wachifundo ndi wokonda kuchereza alendo. Ngati mutatsatira chitsanzo cha Lidiya, inunso mungapeze anzanu abwino.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena