Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • yp2 tsamba 166
  • Chitsanzo Chabwino—Mkazi Wamasiye Wosauka

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chitsanzo Chabwino—Mkazi Wamasiye Wosauka
  • Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri
  • Nkhani Yofanana
  • Mkazi Wamasiye wa ku Zarefati Anadalitsidwa Chifukwa cha Chikhulupiriro
    Nsanja ya Olonda—2014
  • Mwana wa Mayi Wamasiye Anaukitsidwa
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga
    Nsanja ya Olonda—2007
  • “Muzitsatira Mapazi Ake Mosamala Kwambiri”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2021
Onani Zambiri
Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri
yp2 tsamba 166

Chitsanzo Chabwino​—Mkazi Wamasiye Wosauka

Yesu ali pa kachisi anaona gulu la anthu olemera akuponya ndalama zawo moponyamo zopereka. Kenako, anaona mkazi wina wamasiye wosauka akuponya “timakobili tiwiri tating’ono.” (Luka 21:2) Yesu anamuyamikira kwambiri mkaziyo chifukwa cha kuwolowa manja kwake. Chifukwa chiyani? Anthu ena onsewo anaponyamo ‘zimene anatapa pa zochuluka zimene anali nazo, koma mayiyo, mu umphawi wake, anaponya zonse zimene anali nazo, inde zonse zochirikiza moyo wake.’—Maliko 12:44.

Kodi inu mumaona zinthu ngati mmene mayiyu ankaonera? Kodi ndinu wofunitsitsa kugwiritsa ntchito nthawi ndiponso ndalama zanu potumikira Mulungu? Mofanana ndi mkazi wamasiye wosaukayu, mungapereke ndalama kapena kugwira nawo ntchito yosamalira malo olambirira Yehova. Mungagwiritsenso ntchito nthawi ndi ndalama zanu pothandiza ena kuphunzira za Yehova Mulungu. Yehova anaona ndalama zochepa zimene mkazi wamasiyeyo anapereka kuti zithandize pantchito yake ndipo anasangalala nazo. Nanunso, Mulungu adzasangalala nanu ndiponso adzakuthandizani ngati cholinga chanu chachikulu pamoyo ndi kuchita chifuniro chake.—Mateyo 6:33.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena