Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • scl tsamba 120-122
  • Yesu Khristu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu Khristu
  • Malemba Othandiza pa Moyo wa Chikhristu
Malemba Othandiza pa Moyo wa Chikhristu
scl tsamba 120-122

Yesu Khristu

Kodi ndi njira yapadera iti imene Yehova amakwaniritsira chifuniro chake kudzera mwa Yesu?

Mac 4:12; 10:43; 2Ak 1:20; Afi 2:9, 10

Onaninso Miy 8:22, 23, 30, 31; Yoh 1:10; Chv 3:14

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Mt 16:13-17​—Mtumwi Petulo anayankha kuti Yesu ndi Khristu, Mwana wa Mulungu

    • Mt 17:1-9​—Yesu anasintha maonekedwe ake pamaso pa atumwi ake atatu ndipo iwo anamva Yehova akunena kuti Yesu ndi Mwana Wake

Ndi zinthu ziti zimene zimachititsa kuti Yesu akhale wosiyana ndi anthu ena onse?

Yoh 8:58; 14:9, 10; Akl 1:15-17; 1Pe 2:22

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Mt 21:1-9​—Yesu akulowa mu Yerusalemu atakwera bulu anakwaniritsa ulosi wakuti ndi Mesiya, Mfumu yosankhidwa ndi Yehova

    • Ahe 7:26-28​—Mtumwi Paulo anafotokoza mmene Yesu, Mkulu wa Ansembe amasiyanirana ndi akulu a ansembe ena

Kodi zozizwitsa zimene Yesu ankachita zimatiphunzitsa chiyani zokhudza Yesu ndi Atate wake?

Yoh 3:1, 2; 5:36

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Mt 4:23, 24​—Yesu anasonyeza kuti anali wamphamvu kuposa ziwanda ndipo anatha kuchiritsa nthenda yamtundu uliwonse

    • Mt 14:15-21​—Yesu anachulukitsa mikate 5 ndi nsomba ziwiri n’kudyetsa anthu masauzande ambirimbiri mozizwitsa

    • Mt 17:24-27​—Pofuna kusakhumudwitsa anthu, Yesu anachita chozizwitsa n’cholinga choti Petulo apeze ndalama zolipirira msonkho wapakachisi

    • Mko 1:40, 41​—Yesu atagwidwa ndi chifundo, anachiritsa munthu wakhate ndipo umenewu ndi umboni wakuti ndi wofunitsitsa kuchiritsa odwala

    • Mko 4:36-41​—Yesu analetsa mphepo yamkuntho kusonyeza kuti Yehova anamupatsa mphamvu zolamulira mphepo

    • Yoh 11:11-15, 31-45​—Yesu analira mnzake wapamtima Lazaro atamwalira; kenako Yesu anaukitsa Lazaro posonyeza kuti amadana ndi imfa komanso amakhudzidwa ndi ululu umene anthu amamva chifukwa choferedwa

Kodi mfundo yaikulu ya uthenga womwe Yesu ankaphunzitsa inali yotani?

Mt 9:35; Lu 4:43; 8:1; Yoh 18:37

Kodi ndi makhalidwe ena ati omwe Yesu anasonyeza ali padzikoli? Onani mmene anasonyezera kuti anali . . .

Wofikirika​—Mt 13:2; Mko 10:13-16; Lu 7:36-50

Wachifundo​—Mko 5:25-34; Lu 7:11-15

Wolimba mtima​—Mt 4:2-11; Yoh 2:13-17; 18:1-6

Wodzichepetsa​—Mt 11:29; 20:28; Yoh 13: 1-5; Afi 2:7, 8

Wachikondi​—Yoh 13:1; 14:31; 15:13; 1Yo 3:16

Womvera​—Lu 2:40, 51, 52; Ahe 5:8

Wanzeru​—Mt 12:42; 13:54; Akl 2:3

N’chifukwa chiyani Yesu anapereka moyo wake? Nanga nsembe yake imatithandiza bwanji?

Mt 20:28; Yoh 3:16; Mac 10:43; 1Yo 4:9, 10

N’chifukwa chiyani tiyenera kusangalala kuti Yesu Khristu akulamulira monga Mfumu kumwamba?

Sl 72:12-14; Da 2:44; 7:13, 14; Chv 12:9, 10

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Sl 45:2-7, 16, 17​—Salimoli likusonyeza kuti Mfumu yosankhidwa ndi Mulungu idzagonjetsa adani ake onse ndipo idzalamulira mogwirizana ndi choonadi, modzichepetsa komanso mwachilungamo

    • Yes 11:1-10​—Yesu akamadzalamulira monga Mfumu, dzikoli lidzakhala paradaiso ndipo kudzakhala mtendere wochuluka

Kodi Yesu adzachita chiyani posachedwapa?

2At 1:7-9; 2:8; Chv 19:11-21

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena