Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w90 9/15 tsamba 32
  • Pamene Agogo Ake Anamwalira

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Pamene Agogo Ake Anamwalira
  • Nsanja ya Olonda​—1990
Nsanja ya Olonda​—1990
w90 9/15 tsamba 32

Pamene Agogo Ake Anamwalira

Nakubala wa ku Virginia Beach, Virginia, analemba motere kuchiyambi kwa chaka chino: “Mwezi watha atate wanga anamwalira. Iwo ndi mwana wanga wamwamuna wamng’ono kwambiri ankakondana kwambiri, mosasamala kanthu za mtunda womwe unali pakati pawo. Pamene ndinamudziŵitsa kuti agogo ake amwalira, iye anayamba kulira momvetsa chisoni.

“Mwamsanga ndinafunafuna katrakiti kakuti Kodi Pali Chiyembekezo Chotani Kaamba ka Akufa Okondedwa? Mwamsanga nditakapeza, pamene nkhope yake inali idakali yonyowa ndi misozi, ndinayamba kumuŵerengera iko. Pamene ndinamaliza, iye anachitako bata. Ndikuthokoza kaamba ka chidziŵitso chamtengo wake choterocho, chomwe chinali chofunikadi panthaŵi yowawitsa imeneyi.”

Mungalandire trakiti yotonthoza imeneyi, limodzi ndi ena, mwakungodzaza ndi kutumiza kapepala kotsatiraka.

Ndingakonde kulandira katrakiti kakuti Kodi Pali Chiyembekezo Chotani Kaamba ka Akufa Okondedwa? limodzi ndi ena. (Kunja kwa Zambia, lemberani ku nthambi ya Watch Tower yakumaloko kaamba ka chidziŵitso. Onani tsamba 2.)

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena