Mamiliyoni Akupita. Kodi Nanunso Mukupita?
Kupita kuti? Kuchikumbukiro cha chaka ndi chaka cha imfa ya Yesu Kristu. Mu 1990 padziko lonse chiwonkhetso cha anthu 9,950,058 anapezekapo. Kodi nchifukwa ninji anthu amapita? Chifukwa cha chimene imfa ya Kristu imatanthauza kwa anthu. Imatanthauza chimasuko chomayandikira ku matenda, kuvutika, ndi imfa. Ngakhale akufa okondedwa adzaukitsidwira ku moyo padziko lapansi lobwezeretsedwa kukhala Paradaiso. Kodi imfa ya Yesu ingabweretse motani madalitso oterowo? Mukuitanidwa kudzapeza mayankho. Mboni za Yehova zikukulandirani kugwirizana nazo m’chochitika chofunika kwambiri chimenechi. Pezekanipo pa Nyumba Yaufumu yapafupi kwambiri ndi kwanu. Chaka chino tsiku lake ndi Loŵeruka, March 30, dzuŵa litaloŵa. Fufuzani ndi Mboni zakumaloko kaamba ka nthaŵi yeniyeni.