Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w96 3/1 tsamba 3
  • ‘Kodi Ndili Wofunika Pamaso pa Mulungu?’

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • ‘Kodi Ndili Wofunika Pamaso pa Mulungu?’
  • Nsanja ya Olonda—1996
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi “Chipangano Chakale” Chinatha Ntchito?
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Tsiku Lofunika Kwambiri
    Nsanja ya Olonda—2003
  • Filipo—Mlaliki Wokangalika
    Nsanja ya Olonda—1999
  • Kodi Kudziwa Mayankho Olondola Kuli Ndi Phindu?
    Nsanja ya Olonda—2012
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—1996
w96 3/1 tsamba 3

‘Kodi Ndili Wofunika Pamaso pa Mulungu?’

“KODI Ndili Wofunika? Kodi Mulungu Amasamala?” Nkhani ya mu Christianity Today inali ndi mutu umenewo. “Ntchito yanga yambiri monga wolemba nkhani yasumikidwa pankhani ya kuvutika,” akutero Philip Yancey, mlembi wa nkhaniyo. “Ndimadzifunsa mafunso amodzimodzi mobwerezabwereza, monga ngati kuti ndikukhudza chironda chakale chimene sichikuchira kwenikweni. Ndimamva kwa omwe amaŵerenga mabuku anga, ndipo nkhani zawo zomvetsa chisoni zimapereka umboni wa zikayiko zanga.”

Mwinamwake inunso munadzifunsapo za chikondwerero cha Mulungu pa moyo wanu. Eya, mwina mumadziŵa Yohane 3:16, amene amanena kuti “Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wake wobadwa yekha.” Kapena munaŵerengapo Mateyu 20:28, amene amanena kuti Yesu anadza “kupereka moyo wake dipo la anthu ambiri.” Ngakhale zili motero mungafunse kuti, ‘Kodi Mulungu amandiona? Kodi amasamala za ine monga munthu pandekha?’ Pali chifukwa chabwino chokhulupirira kuti amatero, monga mmene tidzaonera.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena