Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w03 3/15 tsamba 3
  • Tsiku Lofunika Kwambiri

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tsiku Lofunika Kwambiri
  • Nsanja ya Olonda—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Uthenga wa Yesu Khristu Umakukhudzani Bwanji?
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Yesu Kristu, kupyolera mwa Amene Mulungu Adzawadalitsa Anthu
    Coonadi Cimene Cimatsogolera ku Moyo Wamuyaya
  • Kodi Imfa ya Yesu Imatanthauzanji kwa Inu?
    Nsanja ya Olonda​—1990
  • Yesu Kristu—Kodi Anatumidwa ndi Mulungu?
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2003
w03 3/15 tsamba 3

Tsiku Lofunika Kwambiri

LINALI tsiku limene linasinthiratu tsogolo la anthu kukhala labwino. Palibe tsiku lina limene limakhudza tsogolo la anthu kuposa limeneli. Ndi tsiku limene Yesu anamaliza zonse zimene anabwerera kudzachita padziko lapansi. Atatsala pang’ono kufa pamtengo wozunzirapo, anafuula kuti: “Kwatha.” (Yohane 19:30) Kodi Yesu anabwera kudzatani padziko lapansi?

Baibulo limati: “Mwana wa munthu sanadza kutumikiridwa koma kutumikira, ndi kupereka moyo wake dipo la anthu ambiri.” (Mateyu 20:28) Yesu anapereka moyo wake kuti anthu apulumutsidwe ku uchimo ndi imfa zimene amabadwa nazo. Indedi, “Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wake wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira Iye asatayike, koma akhale nawo moyo wosatha.” (Yohane 3:16) Nsembe ya Yesu ndi yofunikatu kwambiri!

Tsiku la imfa ya Yesu ndi tsiku lofunika kwambiri pa chifukwa chinanso. Patsiku limeneli, Mwana wa Mulungu anaphunzitsa atumwi ake mfundo zabwino zedi zimene zikanawathandiza kukhalabe okhulupirika. Si mmene mawu ake omaliza kwa ophunzirawo anakhudzira mitima yawo! Kodi anawaphunzitsa zotani? Kodi tingapindule chiyani ndi zimene Yesu anawaphunzitsa? Mafunso ameneŵa ayankhidwa mu nkhani yotsatirayi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena