Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wp16 No. 5 tsamba 3
  • Tonse Timafunika Kulimbikitsidwa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tonse Timafunika Kulimbikitsidwa
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Zimene Zingakuthandizeni Mukamakumana ndi Mavuto
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2016
  • Tonthozani Amene ali ndi Chisoni
    Nsanja ya Olonda—2003
  • Tizilimbikitsa Anthu Amene Achitiridwa Zoipa
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
  • Chitonthozo Chochokera kwa “Mulungu wa Chitonthozo Chonse”
    Nsanja ya Olonda—1995
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2016
wp16 No. 5 tsamba 3

NKHANI YA PACHIKUTO | KODI NDI NDANI ANGATITHANDIZE TIKAKHALA PA MAVUTO?

Tonse Timafunika Kulimbikitsidwa

Mayi akuthandiza mwana wake yemwe wavulala

Kodi munayamba mwagwapo nthawi inayake muli mwana? N’kutheka kuti munavulala dzanja kapena bondo. Kodi mukukumbukira zimene mayi anu anachita pokuthandizani? Mwina anatsuka balalo n’kulimanga ndi kansalu. N’zosakayikitsa kuti munalira koma pasanapite nthawi munatonthola chifukwa mwina mayi anu anakukumbatirani ndiponso kukuuzani mawu olimbikitsa. N’zosachita kufunsa kuti pamene munali mwana simunkasowa anthu okulimbikitsani.

Koma munthu akakula mavuto ake amakhalanso aakulu ndipo zimavuta kuti apeze munthu amene angamulimbikitse. Mavuto amene akuluakulu amakumana nawo sangathetsedwe msanga ngati mmene zimakhalira ndi mavuto a ana. Tiyeni tione zitsanzo za mavuto ena amene timakumana nawo.

  • Kodi nthawi ina munachotsedwapo ntchito? Bambo wina dzina lake Julian ananena kuti atachotsedwa ntchito anasokonezeka maganizo kwambiri. Ankadzifunsa kuti, ‘Kodi ndikwanitsa bwanji kumasamalira banja langa? Ndakhala ndikugwira ntchito mwakhama kwa zaka zambiri pakampaniyi, ndiye n’chifukwa chiyani andichotsa ntchito ngati ndine wachabechabe?’

  • Mwinanso mukusowa mtengo wogwira chifukwa chakuti banja lanu linatha. Mayi wina dzina lake Raquel ananena kuti: “Mwamuna wanga anandithawa mwadzidzidzi ndipo panopa padutsa chaka ndi miyezi 6. Zinandipweteka kwambiri moti ngakhale m’thupi sindinkamva bwino. Ndinkachita mantha kuti zindiyambitsira mavuto ena.”

  • N’kutheka kuti mukudwala matenda enaake ndipo zikuoneka kuti simudzachira. Nthawi zina mungamve ngati mmene Yobu ankamvera. Iye anati: “Moyo ndaukana, sindikufuna kukhala ndi moyo mpaka kalekale.” (Yobu 7:16) Mwinanso mumamva ngati mmene bambo wina wazaka za m’ma 80 dzina lake Luis amamvera. Iye anati: “Nthawi zina ndimaona ngati ndikungodikira imfa.”

  • Kapena mukhoza kumafuna kulimbikitsidwa chifukwa wachibale kapena mnzanu anamwalira. Bambo wina dzina lake Robert ananena kuti: “Mwana wanga atamwalira pa ngozi yandege sindinakhulupirire. Kenako ndinayamba kumva ululu waukulu kwambiri wofanana ndi ululu umene Baibulo limauyerekezera ndi umene munthu angamve atalasidwa ndi lupanga lalitali.”—Luka 2:35.

Robert, Luis, Raquel ndi Julian atakumana ndi mavutowa analimbikitsidwa ndi Mulungu wamphamvuyonse, ndipo palibe wina amene akanawalimbikitsa bwino kuposa iyeyo. Kodi Mulunguyo amalimbikitsa bwanji anthu? Nanga kodi inuyo angakulimbikitseni?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena