Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wp17 No. 4 tsamba 3
  • Kodi Munthu Akamwalira Amakakhalanso Ndi Moyo Kwinakwake?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Munthu Akamwalira Amakakhalanso Ndi Moyo Kwinakwake?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
  • Nkhani Yofanana
  • Moyo wa Pambuyo pa Imfa—Kodi Anthu Amakhulupirira Zotani?
    Nsanja ya Olonda—1999
  • Chiyembekezo Chabwino cha Sou
    Nsanja ya Olonda—1996
  • Kawonedwe Kanu ka Moyo kamayambukira Moyo Wanu
    Nsanja ya Olonda​—1990
  • Imfa
    Galamukani!—2015
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
wp17 No. 4 tsamba 3
Mayi akupemphera atagwira kolona kutsogolo kwa makandulo oyaka

Pafupifupi anthu a m’zipembedzo zonse amakhulupirira kuti munthu ali ndi mzimu umene suufa

NKHANI YA PACHIKUTO | KODI BAIBULO LIMANENA ZOTANI PA NKHANI YA IMFA?

Kodi Munthu Akamwalira Amakakhalanso Ndi Moyo Kwinakwake?

ANTHU ali ndi maganizo osiyanasiyana pa zimene zimachitika munthu akamwalira. Ena amaganiza kuti munthu akafa, amakapitirizabe kukhala ndi moyo kwinakwake kapena amasanduka chinachake. Pomwe ena amaganiza kuti munthu akafa amakabadwanso kwina. Ndiye pali enanso amene amakhulupirira kuti munthu akafa, ndiye kuti basi zonse zathera pomwepo.

Mwina inunso muli ndi zimene mumakhulupirira pa nkhaniyi potengera kumene munakulira komanso chikhalidwe chanu. Monga taonera, anthu ali ndi maganizo osiyanasiyana pa nkhani ya zimene zimachitika munthu akamwalira. Ndiye funso n’kumati: ‘Kodi pali munthu kapena buku limene lingatithandize kudziwa zolondola pa nkhaniyi?’

Kwa zaka zambiri atsogoleri azipembedzo akhala akuphunzitsa kuti munthu ali ndi mzimu umene suufa. Pafupifupi anthu a m’zipembedzo zonse zikuluzikulu, monga Chikhristu, Chihindu, Chiyuda komanso Chisilamu, amakhulupirira kuti munthu akafa mzimu wake umapita kudziko la mizimu kapena kumwamba. Pamene Abuda amakhulupirira kuti munthu akafa amabadwanso kambirimbiri mpaka kenako amakhala ndi moyo wopanda nkhawa womwe amautchula kuti Nirvana.

Anthu akupereka chakudya kwa abale awo omwe anamwalira

Ziphunzitso zimenezi zachititsa kuti anthu ambiri padziko lonse azikhulupirira kuti imfa ndi chiyambi cha moyo wina. Ambiri amaona kuti imfa imayenera kuchitika ndithu pa moyo wa munthu, ndipo Mulungu ndi amene anakonza zoti anthu azifa. Koma kodi Baibulo limati chiyani pa nkhaniyi? Tikukupemphani kuti muwerenge nkhani yotsatira kuti mupeze yankho la funsoli. Mungadabwe ndi zimene Baibulo limanena.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena