Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 11/99 tsamba 1
  • Kulalikira Kumatisiyanitsa ndi Ena

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kulalikira Kumatisiyanitsa ndi Ena
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Nkhani Yofanana
  • Mboni za Yehova
    Kukambitsirana za m’Malemba
  • Chipembedzo
    Kukambitsirana za m’Malemba
  • Kodi Ndinu “Odzipereka pa Ntchito Zabwino”?
    Nsanja ya Olonda—2013
  • “Mbiri Yabwino Iyenera Kulalikidwa Choyamba”
    Nsanja ya Olonda—1988
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
km 11/99 tsamba 1

Kulalikira Kumatisiyanitsa ndi Ena

1 Anthu ambiri amafunsa kuti, “Kodi n’chiyani chimapangitsa chipembedzo cha Mboni za Yehova kusiyana ndi zipembedzo zina?” Kodi inuyo mungayankhe bwanji? Mungafotokoze zina mwa zikhulupiriro zathu za m’Baibulo. Koma kodi munayamba mwalingalirapo zofotokozanso mmene utumiki wathu umatisiyanitsira ndi zipembedzo zina?—Mat. 24:14; 28:19, 20.

2 Lerolino, anthu opembedza ochepa okha ndiwo amasonkhezeredwa kuuza ena zikhulupiriro zawo. Amaganiza kuti ndi kokwanira kumvera malamulo a Kaisara, kukhala ndi makhalidwe abwino, kapena kuchitira ena zabwino. Komabe, saganiza kuti akuyenera kuthandiza ena kuphunzira zimene Baibulo limanena pankhani yopeza chipulumutso. Kodi timasiyana nawo bwanji?

3 Utumiki wathu wachangu umasiyana kwambiri ndi zochita za zipembedzo zina. Kwa zaka zoposa 100, Mboni zamakono, motsatira Akristu oyambirira, zakhala zikulalikira uthenga wabwino mwakhama kufikira kumalekezero a dziko lapansi. Cholinga chathu pochita zimenezi ndicho kuthandiza anthu ambiri kuti miyoyo yawo ikhale yogwirizana ndi chifuniro cha Mulungu.—1 Tim. 2:4; 2 Pet. 3:9.

4 Kodi Mbiri Yanu ndi Yotani? Kodi mumadziŵika monga mlaliki wa Mawu a Mulungu wachangu? (Mac. 17:2, 3; 18:25) Chifukwa cha ntchito yanu yolalikira, kodi anansi anu amasiyanitsa mosavuta chipembedzo chawo ndi chanu? Kodi mumadziŵika monga munthu amene amakhala chire kuti auze ena za chiyembekezo chake? Kodi muli ndi chizoloŵezi chopita mu utumiki? Kumbukirani kuti timadzisiyanitsa osati ndi dzina lathu lokha komanso mwa kuchita zimene dzinalo limanena—kuchitira umboni za Yehova.—Yes. 43:10.

5 Kukonda Mulungu ndi anansi athu kumatisonkhezera kuchita ntchito yolalikira. (Mat. 22:37-39) Ndicho chifukwa chake, mofanana ndi Yesu ndi atumwi, tikufuna kugwiritsa ntchito mpata uliwonse kuuza ena uthenga wa Ufumu. Tiyenitu tipitirize kulalikira uthenga wabwino mwachangu kwa amene ali ofuna kumvetsera. Kuchita zimenezi kudzathandiza anthu oona mtima “kuzindikira pakati pa . . . iye wotumikira Mulungu ndi iye wosam’tumikira.”—Mal. 3:18.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena