Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 February tsamba 7
  • February 29–March 6

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • February 29–March 6
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 February tsamba 7

February 29–March 6

ESITERE 1-5

  • Nyimbo Na. 86 ndi Pemphero

  • Mawu Oyamba (Osapitirira 3 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

  • “Esitere Anapulumutsa Anthu a Mulungu”: (10 min.)

    • [Onetsani vidiyo ya Esitere.]

    • Esitere 3:5-9—Hamani ankafuna kupha anthu onse a Mulungu (ia 131 ndime 18-19)

    • Esitere 4:11–17; 5:1-2—Chikhulupiriro cha Esitere chinali champhamvu moti sankaopa kuphedwa (ia 125 ndime 2; 134 ndime 24-26)

  • Kufufuza Mfundo Zothandiza: (8 min.)

    • Esitere 2:15—Kodi Esitere anasonyeza bwanji kuti anali wodzichepetsa komanso wodziletsa? (w06 3/1 9 ndime 7)

    • Esitere 3:2-4—N’chifukwa chiyani Moredekai ankakana kugwadira Hamani? (ia 131 ndime 18)

    • Kodi ndaphunzira chiyani zokhudza Yehova pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

    • Kodi ndi mfundo ziti zimene ndaphunzira mlungu uno zimene ndingazigwiritse ntchito mu utumiki?

  • Kuwerenga Baibulo: Esitere 1:1-15 (Osapitirira 4 min.)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

  • Ulendo Woyamba: (Osapitirira 2 min.) Perekani kabuku kakuti Mverani Mulungu. Muuzeni zimene mudzakambirane mukadzabweranso.

  • Ulendo Wobwereza: (Osapitirira 4 min.) Chitani chitsanzo chosonyeza kuti mwakumananso ndi munthu amene analandira kabuku kakuti Mverani Mulungu ndipo kambiranani tsamba 2 ndi 3. Muuzeni nkhani imene mudzaphunzire pa ulendo wotsatira.

  • Phunziro la Baibulo: (Osapitirira 6 min.) Chitani chitsanzo chosonyeza mukuphunzira ndi munthu yemwe analandira kabuku kakuti Mverani Mulungu. Gwiritsani ntchito tsamba 4 ndi 5 la kabuku kakuti Mverani Mulungu Kuti Mudzapeze Moyo Wosatha. (km 7/12 2-3 ndime 4)

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

  • Nyimbo Na. 71

  • Zofunika pampingo: (10 min.)

  • Fotokozani Mmene Ndandanda Yatsopano ya Misonkhano Yakuthandizirani?: (5 min.) Nkhani yokambirana. Funsani omvera kuti afotokoze mmene ndandanda yatsopanoyi yawathandizira. Alimbikitseni kuti azikonzekera bwino misonkhanoyi kuti azipindula kwambiri.

  • Phunziro la Baibulo la Mpingo: cl mutu 26 ndime 18-23, ndi bokosi tsa. 269 (30 min.)

  • Mfundo Zimene Taphunzira Komanso za Mlungu wa Mawa (3 min.)

  • Nyimbo Na. 149 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena