CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | 1 AKORINTO 10-13
Yehova ndi Wokhulupirika
Ngakhale kuti Yehova akhoza kutichotsera mayesero, nthawi zambiri amapereka “njira yopulumukira.” Iye amachita zimenezi potipatsa zinthu zofunikira kuti tithe kupirira mayesero omwe takumana nawo.
Angatithandize kuti maganizo ndi mtima wathu zikhale m’malo pogwiritsa ntchito Mawu ake, mzimu wake woyera komanso zinthu zauzimu zomwe amatipatsa.—Mat. 24:45; Yoh. 14:16; Aroma 15:4
Akhoza kutitsogolera pogwiritsa ntchito mzimu woyera womwe ungatithandize kukumbukira mfundo komanso zitsanzo za anthu a m’Baibulo. Angatithandizenso kuganizira njira yabwino yomwe tingasankhe.—Yoh. 14:26
Akhozanso kugwiritsa ntchito angelo ake kuti atithandize.—Aheb. 1:14
Angagwiritsenso ntchito abale ndi alongo athu.—Akol. 4:11