Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb20 April tsamba 2-3
  • April 6-12

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • April 6-12
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
  • Timitu
  • MASIKU OMALIZA A UTUMIKI WA YESU KU YERUSALEMU
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
mwb20 April tsamba 2-3

April 6-12

Mwambo Wokumbukira Imfa ya Khristu Udzachitika Lachiwiri pa 7 April, 2020

Chaka chilichonse panyengo ya Chikumbutso, Akhristu ambiri amaganizira chikondi chachikulu chimene Yehova ndi Mwana wake Yesu Khristu anatisonyeza. (Yoh 3:16; 15:13) Gwiritsani ntchito tchati chili m’munsichi kuti mupeze malemba omwe akufotokoza zimene zinachitika m’nthawi yomaliza ya utumiki wa Yesu ku Yerusalemu. Zomwe zinachitikazo zinafotokozedwa m’chigawo 6 cha buku la Yesu​—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo. Kodi chikondi chomwe Mulungu komanso Khristu anakusonyezani chimakulimbikitsani bwanji?​—2Ak 5:14, 15; 1Yo 4:16, 19.

Yesu akukwera kumwamba ndipo ophunzira ake akumuyang’anitsitsa modabwa.

TAYESANI KUCHITA IZI PA KULAMBIRA KWANU KWA PABANJA

Onerani ndi kukambirana mfundo za m’mbali yoyamba ndi yachiwiri ya vidiyo yakuti ‘Mulungu Anamuika Kukhala Ambuye ndi Khristu’​—Mbali Yoyamba ndi Mbali Yachiwiri.

MASIKU OMALIZA A UTUMIKI WA YESU KU YERUSALEMU

Nthawi

Malo

Zimene Zinachitika

Mateyu

Maliko

Luka

Yohane

33 C.E., Nisani 8 (1-2 April, 2020)

Betaniya

Yesu anafika ku Betaniya kutatsala masiku 6 kuti Pasika achitike

11:55–12:1

Nisani 9 (2-3 April, 2020)

Betaniya

Mariya anathira Yesu mafuta m’mutu ndi m’mapazi

26:6-13

14:3-9

12:2-11

Betaniya-Betefage-Yerusalemu

Analowa mu Yerusalemu mwaulemerero, atakwera bulu

21:1-11, 14-17

11:1-11

19:29-44

12:12-19

Nisani 10 (3-4 April, 2020)

Betaniya-Yerusalemu

Anatemberera mtengo wa mkuyu; kenako anayeretsanso kachisi

21:18, 19; 21:12, 13

11:12-17

19:45, 46

Yerusalemu

Ansembe aakulu ndi alembi anakonza chiwembu choti aphe Yesu

11:18, 19

19:47, 48

Mawu a Yehova anamveka; Yesu ananeneratu za imfa yake; Ayuda sanamukhulupirire ndipo zimenezi zinakwaniritsa ulosi wa Yesaya

12:20-50

Nisani 11 (4-5 April, 2020)

Betaniya-Yerusalemu

Anaphunzitsa anthu pogwiritsa ntchito mtengo wa mkuyu womwe unafota

21:19-22

11:20-25

Yerusalemu, kachisi

Anthu anakaikira ulamuliro wa Khristu; fanizo la ana awiri aamuna

21:23-32

11:27-33

20:1-8

Mafanizo: alimi omwe anapha anthu, phwando la ukwati

21:33–22:14

12:1-12

20:9-19

Yesu anayankha mafunso okhudza Mulungu komanso Kaisara, kuuka kwa akufa, lamulo lalikulu kwambiri

22:15-40

12:13-34

20:20-40

Yesu anafunsa anthu ngati Khristu ali mwana wa Davide

22:41-46

12:35-37

20:41-44

Anadzudzula mwamphamvu alembi ndi Afarisi

23:1-39

12:38-40

20:45-47

Anaona mkazi wamasiye akupereka ndalama

12:41-44

21:1-4

Phiri la Maolivi

Ananena za chizindikiro cha kukhalapo kwake

24:1-51

13:1-37

21:5-38

Mafanizo: anamwali 10, matalente, nkhosa ndi mbuzi

25:1-46

Nisani 12 (5-6 April, 2020)

Yerusalemu

Atsogoleri achiyuda anakonza zoti amuphe

26:1-5

14:1, 2

22:1, 2

Yudasi anakonza zomupereka

26:14-16

14:10, 11

22:3-6

Nisani 13 (6-7 April, 2020)

Pafupi ndi Yerusalemu komanso mkati mwake

Anakonzekera Pasika womaliza

26:17-19

14:12-16

22:7-13

Nisani 14 (7-8 April, 2020)

Yerusalemu

Anadya Pasika ndi atumwi ake

26:20, 21

14:17, 18

22:14-18

Anasambitsa mapazi a atumwi ake

13:1-20

Yesu ananena kuti Yudasi ndi yemwe adzamupereke ndipo anamuuza kuti achoke

26:21-25

14:18-21

22:21-23

13:21-30

Anayambitsa mwambo wa Chakudya Chamadzulo cha Ambuye (1Ak 11:23-25)

26:26-29

14:22-25

22:19, 20, 24-30

Ananeneratu kuti Petulo adzamukana komanso kuti atumwi adzabalalika

26:31-35

14:27-31

22:31-38

13:31-38

Analonjeza kuti adzatumiza mthandizi; fanizo la mpesa; anapereka lamulo la chikondi; anapemphera komaliza ndi atumwi ake

14:1–17:26

Getsemane

Anavutika maganizo; anaperekedwa ndi kumangidwa

26:30, 36-56

14:26, 32-52

22:39-53

18:1-12

Yerusalemu

Anafunsidwa mafunso ndi Anasi; anazengedwa mlandu ndi Kayafa, Khoti Lalikulu la Ayuda; Petulo anamukana

26:57–27:1

14:53–15:1

22:54-71

18:13-27

Yudasi amene anapereka Yesu anadzimangirira (Mac 1:18, 19)

27:3-10

Anaonekera kwa Pilato, Herode, kenako anabwereranso kwa Pilato

27:2, 11-14

15:1-5

23:1-12

18:28-38

Pilato anayesetsa kuti amumasule koma Ayuda anasankha kuti awamasulire Baraba; anaweruzidwa kuti aphedwe mochita kupachikidwa pamtengo

27:15-30

15:6-19

23:13-25

18:39–19:16

(cha m’ma 3 koloko madzulo)

Gologota

Anafa atamupachika pamtengo

27:31-56

15:20-41

23:26-49

19:16-30

Yerusalemu

Anatsitsa thupi lake pamtengo n’kukaliika m’manda

27:57-61

15:42-47

23:50-56

19:31-42

Nisani 15 (8-9 April, 2020)

Yerusalemu

Ansembe ndi Afarisi anatseka pamandapo n’kuikapo alonda

27:62-66

Nisani 16 (9-10 April, 2020)

Yerusalemu ndi madera apafupi; Emau

Yesu anaukitsidwa; anaonekera maulendo 5 kwa ophunzira ake

28:1-15

16:1-8

24:1-49

20:1-25

Pambuyo pa Nisani 16

Yerusalemu; Galileya

Anaonekeranso maulendo angapo kwa ophunzira ake (1Ak 15:5-7; Mac 1:3-8); anawalangiza; ndi kuwalamula kuti agwire ntchito yophunzitsa anthu

28:16-20

20:26–21:25

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena