Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb22 January tsamba 7
  • Yehova Amatisonyeza Chikondi Chokhulupirika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yehova Amatisonyeza Chikondi Chokhulupirika
  • Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Timapindula Bwanji ndi Chikondi Chokhulupirika cha Yehova?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2021
  • Kuthandiza Anthu Amene Akhudzidwa Ndi Ngozi Zadzidzidzi
    Kodi Zopereka Zanu Zimagwiritsidwa Ntchito Bwanji?
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani pa Nkhani ya Ngozi Zadzidzidzi?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • N’chifukwa Chiyani Masoka Achilengedwe Achuluka Chonchi?
    Nsanja ya Olonda—2011
Onani Zambiri
Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
mwb22 January tsamba 7
Abale ndi alongo ali ndi thandizo limene alandira panja pa Nyumba ya Ufumu.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Yehova Amatisonyeza Chikondi Chokhulupirika

Yehova amakuonani kuti ndinu wamtengo wapatali. (Yes 43:4) Anafuna kuti mukhale mnzake ndipo anakubweretsani m’gulu lake. Chifukwa chakuti munadzipereka komanso kubatizidwa, ndinu a Yehova. Iye adzakusamalirani monga chuma chake chapadera, ngakhale pamene zinthu zavuta, ndipo adzakusonyezani chikondi chokhulupirika kudzera m’gulu lake.​—Sl 25:10

Tingasonyeze kuyamikira kwambiri chikondi chokhulupirika cha Yehova, tikaona mmene gulu lake lathandizira anthu pa nthawi ya ngozi zam’chilengedwe zimene zachitika posachedwapa.

ONERANI VIDIYO YAKUTI LIPOTI LA KOMITI YA OGWIRIZANITSA LA 2019, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Chithunzi cha muvidiyo yakuti “Lipoti la Komiti ya Ogwirizanitsa la 2019.” Abale a m’Komiti Yothandiza Pakachitika Ngozi Zadzidzidzi akulankhulana ndi abale ndi alongo omwe anakhudzidwa ndi ngozi zam’chilengedwe.

    Kodi Komiti ya Ogwirizanitsa inakonzekeretsa bwanji maofesi a nthambi padziko lonse za mmene angakonzekerere ngozi zosiyanasiyana?

  • Chithunzi cha muvidiyo yakuti “Lipoti la Komiti ya Ogwirizanitsa la 2019.” Abale akumanga nyumba imene inawonongeka ndi ngozi yam’chilengedwe ku Indonesia.

    Kodi gulu la Yehova linapereka bwanji malangizo komanso thandizo ku Indonesia ndi ku Nigeria?

  • Chithunzi cha muvidiyo yakuti “Lipoti la Komiti ya Ogwirizanitsa la 2019.” Nesi ku Africa akuyeza wodwala pogwiritsa ntchito kachipangizo koyezera kugunda kwa mtima.

    Kodi n’chiyani chakusangalatsani ndi mmene gulu lachitira zinthu pa nthawi ya mliri wa COVID-19?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena