Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • yb15 tsamba 82-tsamba 85 ndime 2
  • Mfundo Zachidule Zokhudza Dominican Republic

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mfundo Zachidule Zokhudza Dominican Republic
  • Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2015
Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2015
yb15 tsamba 82-tsamba 85 ndime 2
Chithunzi patsamba 82

DOMINICAN REPUBLIC

Mfundo Zachidule Zokhudza Dominican Republic

Mapu patsamba 83

Mmene Dzikoli Lilili: Mbali yaikulu pachilumba cha Hispaniola ili m’dziko la Dominican Republic, ndipo mbali yotsalayo ili m’dziko la Haiti. M’dziko la Dominican Republic muli nkhalango, mapiri ataliatali, madambo komanso zipululu. Phiri lalitali kwambiri m’dzikoli ndi la Pico Duarte, ndipo ndi lalitali mamita 3,175. M’madera ambiri a m’mbali mwa nyanja muli mchenga woyera bwino. M’madera a mkatikati mwa dzikoli muli zigwa zachonde, monga chigwa chotchedwa Cibao.

Anthu: Anthu ambiri m’dzikoli ndi makaladi amene makolo awo anachokera ku Ulaya ndi ku Africa. M’dzikoli mulinso anthu a mitundu ina koma ambiri ndi ochokera ku Haiti.

Chilankhulo: Anthu ambiri m’dzikoli amalankhula Chisipanishi.

Chithunzi pamasamba 84, 85

Abale ndi alongo akucheza

Ntchito Zawo: Chuma chambiri m’dzikoli chimachokera ku migodi, shuga, khofi ndiponso fodya. Koma chaposachedwapa, ndalama zambiri zikupezeka kuchokera ku ntchito zokopa alendo komanso ku makampani opanga zinthu zosiyanasiyana.

Nyengo: Nyengo ya m’dzikoli imakhala yabwino chifukwa nthawi zambiri kumatentha madigiri pafupifupi 25. Nayonso mvula imagwa bwino kwambiri. Chaka chilichonse, kumadera akumapiri kumagwa mvula yoposa mamilimita 2,032, koma kumadera ena imagwa mamilimita pafupifupi 760. Nthawi zina m’dzikoli mumachitika mphepo ndi mvula yamkuntho.

Chikhalidwe: M’dzikoli anthu amadalira mpunga, nyemba ndiponso ndiwo zamasamba. Anthu a m’dzikoli amakondanso nsomba, zipatso, tsabola ndiponso nthochi zophika. Zina mwa zakudya zimenezi amazisakaniza n’kuphika chakudya chimene anthu ambiri amakonda, chomwe amachitchula kuti La Bandera Dominicana (kutanthauza mbendera ya ku Dominican). Anthu a m’dzikoli amakondanso mpira, nyimbo ndiponso kuvina. Poimba, amakonda kugwiritsa ntchito gitala, ng’oma, zitoliro ndiponso mangolongondo.

KUKULA KWAKE (square miles)

18,792 (48,671 sq km)

KULI ANTHU

10,404,000

OFALITSA MU 2014

38,161

ALIYENSE AFUNIKA KUPHUNZITSA ANTHU

273

OPEZEKA PA CHIKUMBUTSO MU 2014

132,760

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena