Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwbq nkhani 30
  • N’chifukwa Chiyani Mulungu Sayankha Mapemphero Ena?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • N’chifukwa Chiyani Mulungu Sayankha Mapemphero Ena?
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Yankho la m’Baibulo
  • Pemphero Lingakuthandizeni Kukhala pa Ubwenzi ndi Mulungu
    Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
  • Mmene Mungapemphelere ndi Kumvedwa
    Coonadi Cimene Cimatsogolera ku Moyo Wamuyaya
  • Mapemphero Amene Amayankhidwa
    Nsanja ya Olonda—1988
  • Mmene Mungapezere Chithandizo Kupyolera mwa Pemphero
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
Onani Zambiri
Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
ijwbq nkhani 30

N’chifukwa Chiyani Mulungu Sayankha Mapemphero Ena?

Yankho la m’Baibulo

Mulungu sayankha mapemphero ena. Taonani mfundo ziwiri zotsatirazi zimene zimachititsa kuti Mulungu asayankhe mapemphero a anthu ena.

1. Kupempha zinthu zosagwirizana ndi zimene Mulungu akufuna

Mulungu sayankha mapemphero osagwirizana ndi mfundo zake zimene zili m’Baibulo. (1 Yohane 5:14) Mwachitsanzo, Baibulo limanena kuti tiyenera kupewa mtima wadyera. Juga imalimbikitsa mtima wadyera. (1 Akorinto 6:9, 10) Choncho, Mulungu sangayankhe ngati mukupemphera kuti muwine pa mpikisano kapena juga. Mulungu samangochita chilichonse chimene munthu amafuna. Ndipotu tiyenera kuyamikira zimenezi. Izi zili choncho chifukwa bwenzi tikuopa kuti anthu ena angathe kumupempha ali ndi zolinga zoipa.—Yakobo 4:3.

2. Ngati amene akupempherayo samvera Mulungu mwadala

Mulungu samayankha mapemphero a anthu amene amachita zoipa mwadala. Mwachitsanzo, Mulungu anauza anthu amene ankati akumutumikira koma samumvera mwadala, kuti: “Ngakhale mupereke mapemphero ambiri, ine sindimvetsera. Manja anu adzaza magazi amene mwakhetsa.” (Yesaya 1:15) Koma anthuwo akanasiya zoipa zomwe ankachita n’kukonza ubwenzi wawo ndi Mulungu, iye akanayamba kumvetsera mapemphero awo.—Yesaya 1:18.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena